< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Mon fils, si tu t'engages pour un ami, tu livres ta main à un ennemi;
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
car les lèvres de l'homme sont pour lui un filet très fort, et il est pris par les lèvres de sa propre bouche.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Fais, ô mon fils, ce que je te recommande, et veille à te sauver; à cause de ton ami, tu t'es mis entre les mains des méchants; hâte-toi de t'affranchir, et stimule l'ami pour qui tu as répondu.
4 Usagone tulo, usawodzere.
N'accorde point de sommeil à tes yeux, ni d'assoupissement à tes paupières,
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
pour te sauver comme un daim des filets, et comme un oiseau du piège.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Va voir la fourmi, ô paresseux; regarde, et sois envieux de ses voies, et deviens plus sage qu'elle.
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
Car elle n'a ni laboureurs, ni maîtres, ni personne qui la contraigne.
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
Cependant elle prépare l'été sa nourriture, et en fait d'abondants magasins au temps de la moisson. Ou bien encore va voir l'abeille, et apprends comme elle est industrieuse, et comme son industrie est digne de nos respects; car les rois et les infirmes usent, pour leur santé, des fruits de son labeur. Or elle est glorieuse et désirée de tous, et, si chétive qu'elle soit, on l'honore, parce qu'elle apprécie la sagesse.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Jusques à quand, ô paresseux, resteras-tu couché? Quand sortiras-tu de ton sommeil?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Tu dors un moment, un moment tu t'assieds, tu t'assoupis un peu, tu te tiens un moment les bras croisés,
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
et cependant arrive sur toi la pauvreté comme un dangereux voyageur, et le besoin comme un agile courrier. Mais si tu es actif, la moisson te viendra comme une fontaine, et l'indigence s'enfuira comme un courrier hors de service.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
L'homme insensé et pervers chemine en une voie qui n'est point bonne.
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
Mais il approuve de l'œil, il fait signe du pied, il enseigne par le mouvement de ses doigts.
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
Son cœur pervers pense à mal; en tout temps un tel homme porte le trouble dans la cité.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
À cause de cela, soudain arrivera sa perte; ce sera une chute, une ruine sans remède.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Il se réjouit de toutes les choses que hait le Seigneur; aussi sera-t-il brisé à cause de l'impureté de son âme.
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
Son œil est superbe, sa langue inique; sa main verse le sang du juste;
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
et son cœur roule de mauvais desseins, et ses pieds courent vers le mal.
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
Témoin injuste, il fomente des faussetés, et soulève des discordes entre frères.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Ô mon fils, garde les lois de ton père, et ne rejette pas les préceptes de ta mère.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Tiens-les toujours attachés à ton âme; mets-les comme un collier autour de ton cou.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
Partout où tu iras, porte-les, et qu'ils soient avec toi; et quand tu dormiras, qu'ils te gardent, afin qu'à ton réveil ils s'entretiennent avec toi.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
Les commandements de la loi sont une lampe, une lumière; c'est la voie de vie, c'est la correction et la discipline,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
qui te garderont de la femme mariée et des artifices de la langue étrangère.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Que la convoitise de sa beauté ne triomphe pas de toi; ne te laisse pas prendre par tes yeux, ni ravir par ses paupières.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
Car la courtisane ne coûte que le prix d'un pain; la femme mariée prends les âmes des hommes qui ont tant de prix.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Qui cachera du feu, dans son sein sans brûler sa tunique?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Qui marchera sur des charbons ardents sans se brûler les pieds?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Tel est celui qui a commerce avec la femme mariée; il ne sera point disculpé, non plus que celui qui l'aura touchée.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Il n'est pas étonnant qu'un voleur se cache dans la grange; car il vole pour rassasier son âme affamée;
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
et s'il est pris, il rendra au centuple; et, dût-il donner tout ce qu'il possède, il se sauvera lui-même
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
mais l'adultère, à cause de l'indigence de son cœur, a causé la perte de son âme;
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
il supportera les hontes et les douleurs, et son opprobre ne sera point effacé dans les siècles des siècles.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Car l'âme de l'époux est pleine de jalousie; il ne l'épargnera pas le jour du jugement.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Nul, au prix d'une rançon, n'éteindra sa haine, et il n'est point de dons si nombreux qui puissent l'apaiser.

< Miyambo 6 >