< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Mia filo! se vi garantiis por via proksimulo Kaj donis vian manon por aliulo,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
Tiam vi enretiĝis per la vortoj de via buŝo, Kaptiĝis per la vortoj de via buŝo.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Tiam, mia filo, agu tiel kaj saviĝu, Ĉar vi falis en la mano de via proksimulo: Iru, vigliĝu, kaj petegu vian proksimulon;
4 Usagone tulo, usawodzere.
Ne lasu viajn okulojn dormi Kaj viajn palpebrojn dormeti;
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Savu vin, kiel gazelo, el la mano, Kaj kiel birdo el la mano de la birdokaptisto.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Iru al la formiko, vi maldiligentulo; Rigardu ĝian agadon, kaj saĝiĝu.
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
Kvankam ĝi ne havas estron, Nek kontrolanton, nek reganton,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
Ĝi pretigas en la somero sian panon, Ĝi kolektas dum la rikolto sian manĝon.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Ĝis kiam, maldiligentulo, vi kuŝos? Kiam vi leviĝos de via dormo?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Iom da dormo, iom da dormeto, Iom da kunmeto de la manoj por kuŝado;
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
Kaj venos via malriĉeco kiel rabisto, Kaj via senhaveco kiel viro armita.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
Homo sentaŭga, homo malbonfarema, Iras kun buŝo malica,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
Donas signojn per la okuloj, aludas per siaj piedoj, Komprenigas per siaj fingroj;
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
Perverseco estas en lia koro, li intencas malbonon; En ĉiu tempo li semas malpacon.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
Tial subite venos lia pereo; Li estos rompita subite, kaj neniu lin sanigos.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Jen estas ses aferoj, kiujn la Eternulo malamas, Kaj sep, kiujn Li abomenegas.
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
Arogantaj okuloj, mensogema lango, Kaj manoj, kiuj verŝas senkulpan sangon,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
Koro, kiu preparas malbonfarajn intencojn, Piedoj, kiuj rapidas kuri al malbono,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
Falsa atestanto, kiu elspiras mensogojn; Kaj tiu, kiu semas malpacon inter fratoj.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Konservu, mia filo, la ordonon de via patro, Kaj ne forĵetu la instruon de via patrino.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Ligu ilin por ĉiam al via koro, Volvu ilin sur vian kolon.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
Kiam vi iros, ili gvidos vin; Kiam vi kuŝiĝos, ili vin gardos; Kaj kiam vi vekiĝos, ili parolos kun vi.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
Ĉar moralordono estas lumingo, kaj instruo estas lumo, Kaj edifaj predikoj estas vojo de vivo,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
Por gardi vin kontraŭ malbona virino, Kontraŭ glata lango de fremdulino.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Ne deziregu en via koro ŝian belecon, Kaj ne kaptiĝu per ŝiaj palpebroj.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
Ĉar la kosto de publikulino estas nur unu pano; Sed fremda edzino forkaptas la grandvaloran animon.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Ĉu iu povas teni fajron en sia sino tiel, Ke liaj vestoj ne brulu?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Ĉu iu povas marŝi sur ardantaj karboj, Ne bruligante siajn piedojn?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Tiel ankaŭ estas kun tiu, kiu venas al la edzino de sia proksimulo; Neniu, kiu ŝin ektuŝas, restas sen puno.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Oni ne faras grandan honton al ŝtelanto, Se li ŝtelas por sin satigi, kiam li malsatas;
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
Kaj kiam oni lin kaptas, li pagas sepoble; La tutan havon de sia domo li fordonas.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Sed kiu adultas kun virino, tiu estas sensaĝa; Tiu, kiu faras tion, pereigas sian animon;
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
Batojn kaj malhonoron li ricevas, Kaj lia honto ne elviŝiĝas;
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Ĉar furiozas la ĵaluzo de la edzo; Kaj li ne indulgas en la tempo de la venĝo.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
Li rigardas nenian kompenson, Kaj li ne akceptas, se vi volas eĉ multe donaci.

< Miyambo 6 >