< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
My son, if you have become collateral for your neighbor, if you have struck your hand in pledge for a stranger;
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
You are trapped by the words of your mouth. You are ensnared with the words of your mouth.
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
Do this now, my son, and deliver yourself, seeing you have come into the hand of your neighbor. Go, humble yourself. Press your plea with your neighbor.
4 Usagone tulo, usawodzere.
Give no sleep to your eyes, nor slumber to your eyelids.
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
Free yourself, like a gazelle from the hand of the hunter, like a bird from the snare of the fowler.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Go to the ant, you sluggard. Consider her ways, and be wise;
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
which having no chief, overseer, or ruler,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
provides her bread in the summer, and gathers her food in the harvest.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
How long will you sleep, sluggard? When will you arise out of your sleep?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
A little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep:
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
so your poverty will come as a robber, and your scarcity as an armed man.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
A worthless person, a man of iniquity, is he who walks with a perverse mouth;
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
who winks with his eyes, who signals with his feet, who motions with his fingers;
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
in whose heart is perverseness, who devises evil continually, who always sows discord.
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
Therefore his calamity will come suddenly. He will be broken suddenly, and that without remedy.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
There are six things which the LORD hates; yes, seven which are an abomination to him:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
haughty eyes, a lying tongue, hands that shed innocent blood;
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
a heart that devises wicked schemes, feet that are swift in running to mischief,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
a false witness who utters lies, and he who sows discord among brothers.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
My son, keep your father's commandment, and do not forsake your mother's teaching.
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
Bind them continually on your heart. Tie them around your neck.
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
When you walk, it will lead you. When you sleep, it will watch over you. When you awake, it will talk with you.
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
For the commandment is a lamp, and the Law is light. Reproofs of instruction are the way of life,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
to keep you from the immoral woman, from the flattery of the foreign woman.
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Do not lust after her beauty in your heart, neither let her captivate you with her eyelids.
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
For a prostitute reduces you to a piece of bread. The adulteress hunts for your precious life.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Can a man scoop fire into his lap, and his clothes not be burned?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Or can one walk on hot coals, and his feet not be scorched?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
So is he who goes in to his neighbor's wife. Whoever touches her will not be unpunished.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Men do not despise a thief, if he steals to satisfy himself when he is hungry:
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
but if he is found, he must repay seven times. He shall give all the wealth of his house.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
He who commits adultery with a woman is void of understanding. He who does it destroys his own soul.
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
He will get wounds and dishonor. His reproach will not be wiped away.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
For jealousy arouses the fury of the husband. He won't spare in the day of vengeance.
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
He won't regard any ransom, neither will he rest content, though you give many gifts.

< Miyambo 6 >