< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
Min Søn: har du borget for din næste og givet en anden Håndslag,
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
er du fanget ved dine Læber og bundet ved Mundens Ord,
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
gør så dette, min Søn, og red dig, nu du er kommet i Næstens Hånd: Gå hen uden Tøven, træng ind på din Næste;
4 Usagone tulo, usawodzere.
und ikke dine Øjne Søvn, ej heller dine Øjenlåg Hvile,
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
red dig som en Gazel af Snaren, som en Fugl af Fuglefængerens Hånd.
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Gå hen til Myren, du lade, se dens Færd og bliv viis.
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
Skønt uden Fyrste, Foged og Styrer,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
sørger den dog om Somren for Æde og sanker sin Føde i Høst.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
Hvor længe vil du ligge, du lade, når står du op af din Søvn?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
Lidt Søvn endnu, lidt Blund, lidt Hvile med samlagte Hænder:
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
som en Stimand kommer da Fattigdom over dig, Trang som en skjoldvæbnet Mand.
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
En Nidding, en ussel Mand er den, som vandrer med Falskhed i Munden,
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
som blinker med Øjet, skraber med Foden og giver Tegn med Fingrene,
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
som smeder Rænker i Hjertet og altid kun ypper Kiv;
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
derfor kommer hans Undergang brat, han knuses på Stedet, kan ikke læges.
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
Seks Ting hader HERREN, syv er hans Sjæl en Gru:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
Stolte Øjne, Løgnetunge, Hænder, der udgyder uskyldigt Blod,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
et Hjerte, der udtænker onde Råd, Fødder, der haster og iler til ondt,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
falsk Vidne, der farer med Løgn, og den, som sætter Splid mellem Brødre.
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
Min Søn, tag Vare på din Faders Bud, opgiv ikke din Moders Belæring,
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
bind dem altid på dit Hjerte, knyt dem fast om din Hals;
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
på din Vandring lede den dig, på dit Leje vogte den dig, den tale dig til, når du vågner;
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
thi Budet er en Lygte, Læren Lys, og Tugtens Revselse Livets Vej
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
for at vogte dig for Andenmands Hustru, for fremmed Kvindes sleske Tunge!
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
Attrå ej i dit Hjerte hendes Skønhed, hendes Blik besnære dig ej!
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
Thi en Skøge får man blot for et Brød, men Andenmands Hustru fanger dyrebar Sjæl.
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
Kan nogen bære Ild i sin Brystfold, uden at Klæderne brænder?
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
Kan man vandre på glødende Kul, uden at Fødderne svides?
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
Så er det at gå ind til sin Næstes Hustru; ingen, der rører hende, slipper for Straf.
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
Ringeagter man ikke Tyven, når han stjæler fot at stille sin Sult?
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
Om han gribes, må han syvfold bøde og afgive alt sit Huses Gods.
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
Afsindig er den, der boler med hende, kun en Selvmorder handler så;
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
han opnår Hug og Skændsel, og aldrig udslettes hans Skam.
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
Thi Skinsyge vækker Mandens Vrede, han skåner ikke på Hævnens Dag;
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
ingen Bøde tager han god; store Tilbud rører ham ikke.

< Miyambo 6 >