< Miyambo 6 >

1 Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
我兒,你如果為你的朋友作保,或為外人擊掌;
2 ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
你如果為你口中說的話所連累,為你口中的言詞所束縛,
3 Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
那麼,我兒,你既然已陷在你友人的手中,你就該逃脫,該這樣做:火速前去,央求你的友人,
4 Usagone tulo, usawodzere.
不要合上眼睛睡覺,也不要垂下眼瞼假寐,
5 Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
應急速解救自己,如羚羊掙脫羅網,飛鳥逃脫獵人的圈套。
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
懶漢,你去看看螞蟻,觀察牠的作風,便可得些智識:
7 Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
牠沒有領袖,沒有監督,沒有君王,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
但在夏天卻知準備食糧,在秋收時積貯養料。
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
懶漢,你要睡到幾時,你幾時纔睡醒﹖「
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
再睡片刻,再假寐片刻,再抱臂躺臥片刻! 」
11 umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
這樣貧窮就要如同竊賊,困乏也要如同武士,向你侵襲。
12 Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
無賴與惡徒,行事滿口欺詐;
13 amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
他以眼傳神,以腳示意,以手指東畫西。
14 amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
他存心不良,常蓄意惹事生非。
15 Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
為此,他的喪亡必突然來臨,霎時間全被毀滅,無法挽救。
16 Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
上主憎恨的事,共有六件,連他心裏最厭惡的事,共有七件:
17 maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
傲慢的眼睛,撒謊的舌頭,流無i辜者血的手,
18 mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
策劃陰謀的心,疾趨行惡的腳,
19 mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
說謊的假見證,和在兄弟間搬弄事非的人。
20 Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
我兒,應堅守你父親的命令,不要放棄你母親的教訓;
21 Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
應將二者常刻在你心中,繫在你的頸項上。
22 Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
她們在你行路時引領你,在你躺臥時看護你;在你醒來時與你交談。
23 Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
因為父命是盞燈,母教是光明,嚴格的勸告是生命的道路,
24 kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
使你遠避惡意的女人,離開淫婦阿諛的言詞,
25 Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
不讓你的心貪戀她的美色,不讓她的秋波迷惑你,
26 paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
因為娼妓所求的只是一塊餅,有夫之婦卻獵取寶貴的生命。
27 Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
人豈能懷中藏火,而不燒毀自己的衣服﹖
28 Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
人豈能在火炭上行走,而不灼傷自己的腳﹖
29 Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
與他人妻子通姦的人就是這樣:凡接近她的,必難免受罰。
30 Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
盜賊若因饑餓行竊以果腹,人都不鄙視他;
31 Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
但若被擒獲了,他仍須七倍償還,交出家中所有的財物。
32 Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
與婦人通姦的人,實屬愚眛,他這樣做,卻是毀滅自己。
33 Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
他必遭受可恥的打擊,並且他的恥辱,永不得拭去,
34 Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
因為妒火能激怒男人,使他在報復時,決不留情;
35 Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.
任何的賠償,他都不理睬;即便你多送禮品,他也不肯罷休。

< Miyambo 6 >