< Miyambo 5 >
1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Hijo mío, presta atención a mi sabiduría; deja que tu oído se vuelva a mi enseñanza:
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
para que seas gobernado por un propósito sabio, y tus labios mantengan el conocimiento.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Porque la miel está cayendo de los labios de la mujer extraña, y su voz es más suave que el aceite;
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
Pero su fin es amargo como el ajenjo, y afilado como una espada de dos filos;
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
Sus pies descienden a la muerte, y sus pasos al inframundo; (Sheol )
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Ella nunca mantiene su mente en el camino de la vida; sus caminos son inciertos, ella no tiene conocimiento.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Escúchenme, hijos míos, y no guarden mis palabras de ustedes.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Vete lejos de ella, no te acerques a la puerta de su casa;
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
Por temor a dar tu honor a los demás, y tu riqueza a los hombres extraños:
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
Y los hombres extraños se llene con tus riquezas, y el fruto de tu trabajo ir a la casa de los demás;
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
Y estarás lleno de dolor al final de tu vida, cuando tu carne y tu cuerpo se envejezca;
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
Y dirás: ¿Cómo fue la enseñanza odiada por mí, y mi corazón no valoró el entrenamiento?
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
¡No presté atención a la voz de mis maestros, mi oído no se dirigió a los que me guiaban!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Estaba en casi todas las maldades en compañía de la gente.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Deja que el agua de tu cisterna y no la de los demás sea tu bebida y agua fluyendo de tu propia fuente.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Que no fluyan tus manantiales en las calles, ni tus corrientes de agua en los lugares abiertos.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Déjales que sean solo para ti, no para otros hombres contigo.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Deja que la bendición sea en tu fuente; ten gozo en la esposa de tus primeros años.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
Como cierva amorosa y cierva amable, que sus pechos te den siempre deleite; deja que tu pasión sea movida en todo momento por su amor.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
¿Por qué te permites, hijo mío, salir del camino con una mujer extraña, y tomar otra mujer en tus brazos?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Porque los caminos del hombre están delante de los ojos del Señor, y él pone todas sus caminos en la balanza.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
El malvado será tomado en la red de sus crímenes, y encarcelado en las cuerdas de su pecado.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
El llegará a su fin por necesidad de enseñanza; él es tan tonto que irá vagando por el camino erróneo.