< Miyambo 5 >
1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Hijo mío está atento a mi sabiduría, y a mi inteligencia inclina tu oído:
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
Para que guardes mis consejos; y tus labios conserven la ciencia.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Porque los labios de la mujer extraña destilan panal de miel; y su paladar es más suave que el aceite:
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
Mas su fin es amargo como el ajenjo; agudo como espada de dos filos.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
Sus pies descienden a la muerte: sus pasos sustentan el sepulcro. (Sheol )
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Si no pesares el camino de vida, sus caminos son instables: no los conocerás.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Ahora pues, hijos, oídme, y no os apartéis de las razones de mi boca.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Aleja de ella tu camino; y no te acerques a la puerta de su casa.
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
Porque no des a los extraños tu honor; y tus años a cruel.
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
Porque no se harten los extraños de tu fuerza; y tus trabajos estén en casa del extraño:
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
Y gimas en tus postrimerías, cuando se consumiere tu carne y tu cuerpo,
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
Y digas: ¿Cómo aborrecí el castigo; y mi corazón menospreció la reprensión,
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
Y no oí la voz de los que me castigaban; y a los que me enseñaban no incliné mi oído?
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Poco se faltó para que no cayese en todo mal, en medio de la compañía y de la congregación.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Bebe el agua de tu cisterna, y las corrientes de tu pozo.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Derrámense por de fuera tus fuentes: en las plazas los ríos de tus aguas.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Sean para ti solo, y no para los extraños contigo.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Será bendito tu manadero; y alégrate de la mujer de tu mocedad.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
Cierva amada, y graciosa cabra; sus pechos te hartarán en todo tiempo; y de su amor andarás ciego de continuo.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
¿Y por qué andarás ciego, hijo mío, con la ajena, y abrazarás el seno de la extraña?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Pues que los caminos del hombre están delante de los ojos de Jehová, y él pesa todas sus veredas.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Sus iniquidades prenderán al impío; y con las cuerdas de su pecado será detenido.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Él morirá sin castigo; y por la multitud de su locura errará.