< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Ndodana yami, nanzelela ukuhlakanipha kwami, ulalele kuhle amazwi ami alombono,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
ukuze uhlale ukwazi ukukhetha okuqondileyo lokuze izindebe zakho zigcine ulwazi.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Phela izindebe zesifebekazi zithonta uluju, lenkulumo yaso iyatshelela kulamafutha;
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
kodwa ekucineni iyababa ingathi yinyongo, ibukhali njengenkemba esika nxa zombili.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Inyawo zaso zehlela ekufeni; izinyathelo zaso ziqonda nta elibeni. (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Kasikhathali ukuthi kuphilwa njani; izindlela zaso ziyazombeleza, kodwa kasikuboni lokho.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Ngalokho-ke, madodana ami, ngilalelani; lingaphambuki kulokho engikukhulumayo.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Hambani ngendlela ekhatshana kwaso, lingasondeli emnyango wendlu yaso,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
funa unikele kwabanye amandla akho wonke lobudala bakho kulowo olesihluku,
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
funa abemzini bazitike ngenotho yakho lokusebenza kwakho kunothise umuzi wenye indoda.
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
Ekupheleni kokuphila kwakho uzabubula, lapho inyama yakho lomzimba wakho sekugugile.
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
Uzakuthi, “Uthi ngangikuzonda yini ukulaywa! Inhliziyo yami yayikuzonda njani ukuqondiswa!
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
Ngangingafuni ukulalela abafundisi bami kumbe ukulalela abeluleki bami.
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Ngacina sengisenkingeni enkulu ngiphakathi kwabantu bakaNkulunkulu.”
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Natha amanzi kowakho umgqomo, amanzi agelezayo kowakho umthombo.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Kambe imifudlana yakho ingayekelwa igelezela emigwaqweni, lezifula zakho zamanzi zigelezele ezinkundleni zabantu na?
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Kazibe ngezakho wena wedwa, ungazabelani labafokazana nje.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Sengathi ungabusiswa umthombo wakho njalo sengathi ungathokoza ngomfazi wobutsha bakho.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
Oyimpalakazi ethandekayo, imbabala ebutshelezi amabele akhe sengathi angakusuthisa lanini, nini lanini ukhangwe luthando lwakhe.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
Kungani ndodana yami, uthunjwa yisifebekazi? Kungani ugona iqolo lomfazi wenye indoda?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Phela izindlela zomuntu zisobala kuThixo, uyazihlola zonke izindlela zakhe.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Izenzo ezimbi zomuntu omubi ziyamthiya; izibopho zesono sakhe zimuthe nko.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Uzabhubha ngoba engalayeki, elahlekiswa yibuphukuphuku bakhe.

< Miyambo 5 >