< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Fili mi, attende ad sapientiam meam, et prudentiae meae inclina aurem tuam,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
ut custodias cogitationes, et disciplinam labia tua conservent. Ne attendas fallaciae mulieris.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
favus enim distillans labia meretricis, et nitidius oleo guttur eius.
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
novissima autem illius amara quasi absinthium, et acuta quasi gladius biceps.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Pedes eius descendunt in mortem, et ad inferos gressus illius penetrant. (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Per semitam vitae non ambulant, vagi sunt gressus eius, et investigabiles.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Nunc ergo fili mi audi me, et ne recedas a verbis oris mei.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Longe fac ab ea viam tuam, et ne appropinques foribus domus eius.
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
Ne des alienis honorem tuum, et annos tuos crudeli.
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
ne forte implentur extranei viribus tuis, et labores tui sint in domo aliena,
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
et gemas in novissimis, quando consumpseris carnes tuas et corpus tuum, et dicas:
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
Cur detestatus sum disciplinam, et increpationibus non acquievit cor meum,
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
nec audivi vocem docentium me, et magistris non inclinavi aurem meam?
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Pene fui in omni malo, in medio ecclesiae et synagogae.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Bibe aquam de cisterna tua, et fluenta putei tui:
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Deriventur fontes tui foras, et in plateis aquas tuas divide.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Habeto eas solus, nec sint alieni participes tui.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Sit vena tua benedicta, et laetare cum muliere adolescentiae tuae:
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
cerva charissima, et gratissimus hinnulus. ubera eius inebrient te in omni tempore, in amore eius delectare iugiter.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
Quare seduceris fili mi ab aliena, et foveris in sinu alterius?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Respicit Dominus vias hominis, et omnes gressus eius considerat.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Iniquitates suas capiunt impium, et funibus peccatorum suorum constringitur.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Ipse morietur, quia non habuit disciplinam, et in multitudine stultitiae suae decipietur.

< Miyambo 5 >