< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
E KUU keiki, e hoolohe mai i ko'u naauao, E haliu mai hoi kou pepeiao i ko'u iko:
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
I malama oe i ke aoia mai, E hoopaa hoi kou mau lehelehe i ka ike.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
No ka mea, o na lehelehe o ka wahine hookamakama he meli ia e kulu ana, A ua oi aku ka pahee o kona waha i ko ka aila.
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
Aka, na awahia kona hope, e like me ka laau awaawa, Oioi hoi o like me ka pahikaua oi lua.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Ke iho iho la kona mau wawae i ka make, E pili ana hoi kona mau kapuwai i ka lua, (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
I ole oe e noonoo i ke ala o ko ola, He loli wale kona noho ana i ole oe e ike aku.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Ano la, e na keiki, hoolohe mai ia'u, Mai haliu ae mai ka olelo aku a kuu waha.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
E hooneenee loa aku i kou hele ana mai ona aku, Mai hookokoke aku oe i ka puka o kona hale:
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
O haawi oe i kou nani i na mea e, A me kon mau makahiki hoi i ka mea aloha ole:
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
O lako hoi na mea e i kou mau mea maikai; A me na hale o ka malihini i kau waiwai;
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
A uwe oe i kou hope, I ka pau ana o kou io a me kou kino;
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
A e olelo hoi, Auwe ko'u inaina aku i ka ike, A me ka hoowahawaha ana o ko'u naau i ke aoia mai!
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
Aole au i hoolohe i ka leo o ka'u mau kumu, Aole hoi i haliu aku ko'u pepeiao i ka poe i ao mai ia'u!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Mai noho au ma na hewa a pau loa, Mawaena o ke anaina a me ka ahakanaka.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
E ia u oe i ka wai noloko ae o kou punawai, A i na waikahe hoi noloko ae o kou kahawai.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
E hu aku iwaho kou mau lokowai, A kahe na auwai ma na alanui.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Nau wale iho no lakou, Aole na ka poe malihini pu me oe.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
E hoomaikaiia kou punawai; A e olioli oe me ka wahine o kou wa ui.
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
He dia aloha ia a me ka ibeka oluolu; E maona oe i na la a pau i kona waiu, E ana mau oe i kona aloha.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
No ke aha la e ona oe, e kuu keiki, i ka wahine e, A e apo oe i ka wahine a hai ma kou umauma?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
No ka mea, e kau pono ana na maka o Iehova i ka aoao o ke kanaka, E ike ana no hoi i kona mau aoao a pau,
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
E puni ka mea hewa i kona hala iho, E heiia hoi oia i ka hei o kona hewa iho.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
E make oia me ke ao ole ia mai; A e hele hewa oia i ka nui o kona naaupo ana.

< Miyambo 5 >