< Miyambo 5 >
1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Mein Kind, merke auf meine Weisheit; neige dein Ohr zu meiner Lehre,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
daß du behaltest guten Rat und dein Mund wisse Unterschied zu haben.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Denn die Lippen der Hure sind süß wie Honigseim, und ihre Kehle ist glätter denn Öl,
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
aber hernach bitter wie Wermut und scharf wie ein zweischneidig Schwert.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol )
Ihre Füße laufen zum Tod hinunter, ihre Gänge erlangen die Hölle. (Sheol )
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Sie gehet nicht stracks auf dem Wege des Lebens; unstet sind ihre Tritte, daß sie nicht weiß, wo sie gehet.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
So gehorchet mir nun, meine Kinder, und weichet nicht von der Rede meines Mundes!
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Laß deine Wege ferne von ihr sein und nahe nicht zur Tür ihres Hauses,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
daß du nicht den Fremden gebest deine Ehre und deine Jahre dem Grausamen,
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
daß sich nicht Fremde von deinem Vermögen sättigen, und deine Arbeit nicht sei in eines andern Haus,
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
und müssest hernach seufzen, wenn du dein Leib und Gut verzehret hast,
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
und sprechen: Ach, wie habe ich die Zucht gehasset, und mein Herz die Strafe verschmähet,
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
und habe nicht gehorchet der Stimme meiner Lehrer und mein Ohr nicht geneigt zu denen, die mich lehreten!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Ich bin schier in all Unglück kommen vor allen Leuten und allem Volk.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Trinke Wasser aus deiner Grube und Flüsse aus deinem Brunnen.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Laß deine Brunnen herausfließen und die Wasserbäche auf die Gassen.
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Habe du aber sie alleine und kein Fremder mit dir.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Dein Born sei gesegnet, und freue dich des Weibes deiner Jugend!
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
Sie ist lieblich wie eine Hindin und holdselig wie ein Reh. Laß dich ihre Liebe allezeit sättigen, und ergötze dich allewege in ihrer Liebe.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
Mein Kind, warum willst du dich an der Fremden ergötzen und herzest dich mit einer andern?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Denn jedermanns Wege sind stracks vor dem HERRN, und er misset gleich alle ihre Gänge.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Die Missetat des Gottlosen wird ihn fahen, und er wird mit dem Strick seiner Sünde gehalten werden.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Er wird sterben, daß er sich nicht will ziehen lassen, und um seiner großen Torheit willen wird's ihm nicht wohlgehen.