< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Mærk dig, min Søn, min Visdom, bøj til min Indsigt dit Øre,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
at Kløgt må våge øver dig, Læbernes kundskab vare på dig.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Thi af Honning drypper den fremmedes Læber, glattere end Olie er hendes Gane;
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
men til sidst er hun besk som Malurt, hvas som tveægget Sværd;
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
hendes Fødder styrer nedad mod Døden, til Dødsriget stunder hendes Fjed; (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
hun følger ej Livets Vej, hendes Spor er bugtet, hun ved det ikke.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Hør mig da nu, min Søn, vig ikke fra min Munds Ord!
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Lad din Vej være langt fra hende, kom ej hendes Husdør nær,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
at du ikke må give andre din Ære, en grusom Mand dine År.
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
at ikke dit Gods skal mætte fremmede, din Vinding ende i Andenmands Hus,
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
så du gribes af Anger til sidst, når dit Kød og Huld svinder hen,
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
og du siger: "Ak, at jeg hadede Tugt, at mit Hjerte lod hånt om Revselse,
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
så jeg ikke lød mine Læreres Røst, ej bøjed mit Øre til dem, som lærte mig!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
Nær var jeg kommet i alskens Ulykke midt i Forsamling og Menighed!"
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Drik Vand af din egen Cisterne og rindende Vand af din Brønd;
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
lad ej dine Kilder flyde på Gaden, ej dine Bække på Torvene!
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Dig skal de tilhøre, dig alene, ingen fremmed ved Siden af dig!
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Velsignet være dit Væld, og glæd dig ved din Ungdoms Hustru,
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
den elskelige Hind, den yndige Gazel; hendes Elskov fryde dig stedse, berus dig altid i hendes Kærlighed!
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
Hvi beruser du dig, min Søn, i en fremmed og tager en andens Hustru i Favn?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Thi for HERRENs Øjne er Menneskets Veje, grant følger han alle dets Spor;
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
den gudløse fanges af egen Brøde og holdes fast i Syndens Reb;
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
han dør af Mangel på Tugt, går til ved sin store Dårskab.

< Miyambo 5 >