< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
Sine moj, čuj moju mudrost, prigni uho mojoj razboritosti
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
da sačuvaš oprez, da ti usne zadrže znanje.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
Jer s usana žene preljubnice kaplje med i nepce joj je glađe od ulja,
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
ali je ona naposljetku gorka kao pelin, oštra kao dvosjekli mač.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Njene noge silaze k smrti, a koraci vode u Podzemlje. (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
Ona ne pazi na put života, ne mari što su joj staze kolebljive.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Zato me sada poslušaj, sine, i ne odstupaj od riječi mojih usta.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Neka je put tvoj daleko od nje i ne približuj se vratima njezine kuće,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
da drugima ne bi dao svoju slavu i okrutnima svoje godine;
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
da se ne bi tuđinci nasitili tvoga dobra i da tvoja zaslužba ne ode u tuđu kuću;
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
da ne ridaš na koncu kad ti nestane tijela i puti
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
i da ne kažeš: “Oh, kako sam mrzio pouku i kako mi je srce preziralo ukor!
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
I ne slušah glasa svojih učitelja, niti priklonih uho onima što me poučavahu.
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
I umalo ne zapadoh u svako zlo, usred zbora i zajednice!”
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Pij vodu iz svoje nakapnice i onu što teče iz tvoga studenca.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Moraju li se tvoji izvori razlijevati i tvoji potoci teći ulicama?
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Nego neka oni budu samo tvoji, a ne i tuđinaca koji su uza te.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Neka je blagoslovljen izvor tvoj i raduj se sa ženom svoje mladosti:
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
neka ti je kao mila košuta i ljupka gazela, neka te grudi njene opajaju u svako doba, njezina ljubav zatravljuje bez prestanka!
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
TÓa zašto bi se, sine moj, zanosio preljubnicom i grlio tuđinki njedra?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
Jer pred Jahvinim su očima čovjekovi putovi i on motri sve njegove staze.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
Opakoga će uhvatiti njegova zloća i sapet će ga užad njegovih grijeha.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
Umrijet će jer nema pouke, propast će zbog svoje goleme gluposti.

< Miyambo 5 >