< Miyambo 4 >

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Escucha, mis hijos, a la enseñanza de un padre; presta atención para que puedas tener conocimiento:
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
Porque te doy una buena enseñanza; no renuncies al conocimiento que recibes de mí.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Porque yo era un hijo para mi padre, un gentil y único para mi madre.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
Y me dio enseñanza, diciéndome: Guarda mis palabras en tu corazón; guarda mis reglas para que puedas tener vida:
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Obtén sabiduría, obtén verdadero conocimiento; guárdelo en la memoria, no se aparte de las palabras de mi boca.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
No la abandones, y ella te guardará; dale tu amor, y ella te hará a salvo.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
El primer signo de sabiduría es obtener sabiduría; ve, da todo lo que tienes para obtener el verdadero conocimiento.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Ponla en un lugar alto, y serás levantado por ella; Ella te dará honor cuando le des tu amor.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
Ella pondrá una corona de gracia en tu cabeza, dándote un tocado de gloria.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
Escucha, hijo mío, y deja que tu corazón se abra a mis palabras; y larga vida será tuya.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
Te he dado la enseñanza en el camino de la sabiduría, guiando tus pasos en el camino recto.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
Cuando vayas, tu camino no será estrecho, y al correr no tendrás una caída.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Toma el aprendizaje en tus manos, no la dejes ir: mantenla, porque ella es tu vida.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
No sigas el camino de los pecadores, ni andes en el camino de los hombres malos.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Aléjate de él, no te acerques; se apartado de eso, y sigue tu camino.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
Porque no descansan hasta que hayan hecho lo malo; se les quita el sueño si no han sido la causa de la caída de alguien.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
El pan del mal es su alimento, el vino de los actos violentos su bebida.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
Pero el camino de los justos es como la luz de la mañana, cada vez más brillante hasta el día completo.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
El camino de los pecadores es oscuro; ellos no ven la causa de su caída.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
Hijo mío, presta atención a mis palabras; deja que tu oído se vuelva a mis dichos.
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
No deja que se aparten de tus ojos; mantenlos en lo profundo de tu corazón.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
Porque ellos son vida para el que los recibe, y fortaleza para toda su carne.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
Y guarda tu corazón con todo cuidado; entonces tendrás vida.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Aparta de ti una lengua mala, y que los labios falsos estén lejos de ti.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Mantén tus ojos en lo recto, en lo que está frente a ti, mirando directamente hacia ti.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Vigila tu comportamiento; deja que todos tus caminos sean ordenados correctamente.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
No haya vuelta a la derecha ni a la izquierda, aparten sus pies del mal.

< Miyambo 4 >