< Miyambo 4 >
1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Höret, meine Kinder, die Zucht eures Vaters; merkt auf, daß ihr lernet und klug werdet!
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
Denn ich gebe euch eine gute Lehre; verlasset mein Gesetz nicht!
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Denn ich war meines Vaters Sohn, ein zarter und ein einiger vor meiner Mutter,
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
und er lehrete mich und sprach: Laß dein Herz meine Worte aufnehmen; halte meine Gebote, so wirst du leben.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Nimm an Weisheit, nimm an Verstand; vergiß nicht und weiche nicht von der Rede meines Mundes!
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Verlaß sie nicht, so wird sie dich behalten; liebe sie, so wird sie dich behüten.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
Denn der Weisheit Anfang ist, wenn man sie gerne höret und die Klugheit lieber hat denn alle Güter.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Achte sie hoch, so wird sie dich erhöhen und wird dich zu Ehren machen, wo du sie herzest.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
Sie wird dein Haupt schön schmücken und wird dich zieren mit einer hübschen Krone.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
So höre, mein Kind, und nimm an meine Rede, so werden deiner Jahre viel werden.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
Ich will dich den Weg der Weisheit führen, ich will dich auf rechter Bahn leiten,
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
daß, wenn du gehest, dein Gang dir nicht sauer werde, und wenn du läufst, daß du dich nicht anstoßest.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Fasse die Zucht, laß nicht davon; bewahre sie, denn sie ist dein Leben.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
Komm nicht auf der Gottlosen Pfad und tritt nicht auf den Weg der Bösen.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Laß ihn fahren und gehe nicht drinnen; weiche von ihm und gehe vorüber!
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
Denn sie schlafen nicht, sie haben denn übel getan; und sie ruhen nicht, sie haben denn Schaden getan.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
Denn sie nähren sich von gottlosem Brot und trinken vom Wein des Frevels.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
Aber der Gerechten Pfad glänzet wie ein Licht, das da fortgeht, und leuchtet bis auf den vollen Tag.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
Der Gottlosen Weg aber ist wie Dunkel und wissen nicht, wo sie fallen werden.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
Mein Sohn, merke auf mein Wort und neige dein Ohr zu meiner Rede!
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
Laß sie nicht von deinen Augen fahren; behalte sie in deinem Herzen!
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
Denn sie sind das Leben denen, die sie finden, und gesund ihrem ganzen Leibe.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
Behüte dein Herz mit allem Fleiß; denn daraus gehet das Leben.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Tu von dir den verkehrten Mund und laß das Lästermaul ferne von dir sein.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Laß deine Augen stracks vor sich sehen und deine Augenlider richtig vor dir hinsehen.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Laß deinen Fuß gleich vor sich gehen, so gehest du gewiß.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
Wanke weder zur Rechten noch zur Linken; wende deinen Fuß vom Bösen!