< Miyambo 4 >

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Écoutez, fils, l'instruction d'un père. Soyez attentif et sachez comprendre;
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
car je vous donne un apprentissage solide. N'abandonnez pas ma loi.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Car j'étais un fils pour mon père, tendre et enfant unique aux yeux de ma mère.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
Il m'a enseigné, et m'a dit: « Que ton cœur retienne mes paroles. Gardez mes commandements, et vivez.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Obtenez la sagesse. Comprendre. N'oubliez pas, et ne déviez pas des paroles de ma bouche.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Ne l'abandonne pas, et elle te préservera. Aimez-la, et elle vous gardera.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
La sagesse est suprême. Faites preuve de sagesse. Oui, même si cela vous coûte tous vos biens, soyez compréhensif.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Estime-la, et elle t'élèvera. Elle vous fera honneur lorsque vous l'embrasserez.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
Elle donnera à ta tête une guirlande de grâce. Elle vous délivrera une couronne de splendeur. »
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
Écoute, mon fils, et reçois mes paroles. Les années de votre vie seront nombreuses.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
Je vous ai enseigné la voie de la sagesse. Je vous ai conduit dans des chemins droits.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
Quand tu iras, tes pas ne seront pas entravés. Quand vous courrez, vous ne trébucherez pas.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Saisissez fermement l'instruction. Ne la laisse pas partir. Garde-la, car elle est ta vie.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
N'entrez pas dans le chemin des méchants. Ne marchez pas dans la voie des hommes mauvais.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Évitez-le, et ne passez pas à côté. Détournez-vous et passez votre chemin.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
Car ils ne dorment pas s'ils ne font pas le mal. On leur enlève le sommeil, sauf s'ils font tomber quelqu'un.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
Car ils mangent le pain de la méchanceté et boire le vin de la violence.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
Mais le chemin des justes est comme la lumière qui se lève. qui brille de plus en plus jusqu'au jour parfait.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
La voie des méchants est comme les ténèbres. Ils ne savent pas sur quoi ils butent.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
Mon fils, sois attentif à mes paroles. Prêtez l'oreille à mes paroles.
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
Qu'ils ne s'éloignent pas de tes yeux. Gardez-les au centre de votre cœur.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
Car ils sont la vie pour ceux qui les trouvent, et la santé à l'ensemble de leur corps.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
Garde ton cœur avec toute la diligence requise, car de lui jaillit la source de la vie.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Éloigne de toi une bouche perverse. Mettez les lèvres corrompues loin de vous.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Laissez vos yeux regarder droit devant vous. Fixez votre regard directement devant vous.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Faites en sorte que la trajectoire de vos pieds soit de niveau. Que toutes tes voies soient établies.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
Ne vous tournez ni vers la droite ni vers la gauche. Retirez votre pied du mal.

< Miyambo 4 >