< Miyambo 4 >

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Listen to O children [the] correction of a father and be attentive to know understanding.
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
For instruction good I give to you instruction my may not you neglect.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
If a son I was of father my tender and only [child] before mother my.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
And he taught me and he said to me let it hold fast to words my heart your keep commandments my and live.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Acquire wisdom acquire understanding may not you forget and may not you turn aside from [the] utterances of mouth my.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
May not you abandon her and she will keep you love her and she will guard you.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
[is] first Wisdom acquire wisdom and by all acquisition your acquire understanding.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Esteem her and she will exalt you she will honor you if you will embrace her.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
She will put to head your a wreath of grace a crown of beauty she will give you.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
Listen O son my and receive words my so they may increase for you years of life.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
[the] way of Wisdom I taught you I led you in tracks of uprightness.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
When walking you not anyone will hinder step[s] your and if you will run not you will stumble.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Take hold on discipline may not you let go keep her for she [is] life your.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
In [the] path of wicked [people] may not you go and may not you advance in [the] way of evil [people].
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Avoid it may not you pass along on it turn aside from on it and pass on.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
For not they will sleep if not they do harm and it is taken away sleep their if not (they bring injury. *Q(K)*)
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
For they eat [the] bread of wickedness and [the] wine of violence they drink.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
And [the] path of righteous [people] [is] like a light of brightness [which] goes and [which] shines until [the] established [part] of the day.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
[the] way of Wicked [people] [is] like darkness not they know on what? are they stumbling.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
O son my to words my be attentive! to utterances my incline ear your.
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
Do not let them depart from eyes your keep them in [the] midst of heart your.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
For [are] life they to [those who] find them and to all flesh his health.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
More than all guarding guard heart your for [are] from it [the] sources of life.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Remove from yourself crookedness of mouth and deviousness of lips put far away from yourself.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Eyes your before let them look and eyelids your let them look straight before you.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Make level [the] track of foot your and all ways your let them be steadfast.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
May not you turn aside right and left turn aside foot your from evil.

< Miyambo 4 >