< Miyambo 4 >

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Poslouchejte, synové, učení otcova, a pozorujte, abyste poznali rozumnost.
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
Nebo naučení dobré dávám vám, neopouštějtež zákona mého.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
Když jsem byl syn u otce svého mladičký, a jediný při matce své,
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
On vyučoval mne a říkal mi: Ať se chopí výmluvností mých srdce tvé, ostříhej přikázaní mých, a živ budeš.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Nabuď moudrosti, nabuď rozumnosti; nezapomínej, ani se uchyluj od řečí úst mých.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Neopouštějž jí, a bude tě ostříhati; miluj ji, a zachová tě.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
Předně moudrosti, moudrosti nabývej, a za všecko jmění své zjednej rozumnost.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Vyvyšuj ji, a zvýšíť tě; poctí tě, když ji přijmeš.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
Přidá hlavě tvé příjemnosti, korunou krásnou obdaří tě.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
Slyš, synu můj, a přijmi řeči mé, a tak rozmnoží se léta života tvého.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
Cestě moudrosti učím tě, vedu tě stezkami přímými.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
Když choditi budeš, nebude ssoužen krok tvůj, a poběhneš-li, neustrčíš se.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Chopiž se učení, nepouštěj, ostříhej ho, nebo ono jest život tvůj.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
Na stezku bezbožných nevcházej, a nekráčej cestou zlostníků.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Opusť ji, nechoď po ní, uchyl se od ní, a pomiň jí.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
Neboť nespí, leč zlost provedou; anobrž zahánín bývá sen jejich, dokudž ku pádu nepřivodí,
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
Proto že jedí chléb bezbožnosti, a víno loupeží pijí.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
Ale stezka spravedlivých jako světlo jasné, kteréž rozmáhá se, a svítí až do pravého dne.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
Cesta pak bezbožných jako mrákota; nevědí, na čem se ustrčiti mohou.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
Synu můj, slov mých pozoruj, k řečem mým nakloň ucha svého.
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
Nechať neodcházejí od očí tvých, ostříhej jich u prostřed srdce svého.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
Nebo životem jsou těm, kteříž je nalézají, i všemu tělu jejich lékařstvím.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
Přede vším, čehož se stříci sluší, ostříhej srdce svého, nebo z něho pochází život.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Odlož od sebe převrácenost úst, a zlost rtů vzdal od sebe.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Oči tvé ať k dobrým věcem patří, a víčka tvá ať přímě hledí před tebou.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Zvaž stezku noh svých, a všecky cesty tvé ať jsou spraveny.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
Neuchyluj se na pravo ani na levo, odvrať nohu svou od zlého.

< Miyambo 4 >