< Miyambo 4 >
1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
孩子,你們要聽父親的教訓,專心學習明智,
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
因為我把好教訓授給你們,你們不要拋棄我的規勸。
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
我也曾在父親面前作過孝子,在我母親膝下是唯一的嬌兒。
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
我父曾訓誨我說:你應留心牢記我的話,遵守我的命令,好使你生存;
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
你應緊握智慧,握住明智,不要忘記,也不要離棄我口中的教訓:
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
你若不捨棄她,她必護佑你;你若喜愛她,她必看顧你。
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
首先應爭取的是智慧,因此你應尋求智慧,應犧牲一切去爭取明智。
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
你若顯揚智慧,智慧也必顯揚你;你若懷抱她,她也必光榮你:
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
將華冠加在你的頭上,將榮冕賜給你。
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
我兒,你若聽取我的訓言,你必延年益壽。
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
我要教給你智慧的道路,引你走上正直的途徑:
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
這樣,你若行走,你的腳決不會受阻礙;即便你奔馳,也決不致顛仆。
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
你要堅持教訓,切勿把她拋棄;你應保存她,因為她是你的生命。
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
惡人的道路,你不要進去;壞人的途徑,你不要踏入;
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
反應躲避,不經其上;遠遠離去,繞道他往。
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
因為他們不作惡,不能入睡;不使人跌倒,就要失眠。
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
他們吃的是邪惡的餅,飲的是暴虐的酒。
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
但是,義人的途徑,像黎明的曙光,越來越明亮,直至成日中;
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
惡人的道路,卻宛如幽暗,他們不知道,要跌在何處。
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
我兒,你要注意我的訓言,側耳傾聽我的教導;
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
不要讓她離開你的視線,卻要牢記在心中。
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
因為,凡找著她的,必獲得生命;他整個身軀,必獲得健康。
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
在一切之上,你要謹守你的心,因為生命是由此而生。
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
你應摒絕口舌的欺詐,遠避唇舌的乖謬。
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
你的眼睛應向前直視,你的視線應向前集中。
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
你要修平你腳下的行徑,要鞏固你一切的路途。
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
你斷不可左傾右依,務使你的腳遠離邪惡。