< Miyambo 31 >
1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Ty enta’ i Lemoela Mpanjaka, ty onin-drehake nanaren-drene’e aze:
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Anhan ry anako! Anhan ry anake tañ’ ovako ao! Anhan ry anako nafantoko!
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Ko atolo’o aman’ ampela ty haozara’o, ndra amo mpandrotsake mpanjakao o sata’oo.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
Tsy mañeva ty mpanjaka, ry Lemoela, tsy sazo’ i mpanjakay ty mikama divay, ndra o mpamelek’ arivoo ty hilelalela toake;
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
kera hinoñe naho handikoke i liliy vaho hañamengoke ty zo’ o anan-kasotriañeo.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Anjotsò toake ty heta’e, vaho divay ty voretra añ’arofo,
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
angao hinon-dre hañaliñoa’e ty hararaha’e, tsy ho tiahy ka o hasotria’eo.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Manokafa falie hisolo ty moañe, ho ami’ty zo’ o anam-pamàrañe iabio.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Manokafa falie vaho mizakà an-kahiti’e; ambeno ty zo’ o rarake naho mavomavoo.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Ia ty mahaonin-drakemba mañeva? Ie sarotse te amo safirao.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
Atokisa’ ty trom-bali’e, ie tsy ho po-vara.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Hasoa’e fa tsy mañànto, amy ze hene andro fiveloma’e.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Paia’e ty volon-añondry naho ty vinda, vaho an-kafaleañe ty ifanehafa’e am-pitàñe.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Manahake o lakam-pañondrañeo, boak’añe ty añandesa’e mahakama.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Mitroatse te mbe haleñe, hamahañe o keleia’eo, vaho handiva amo anak’ ampata’eo.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Ereñerè’e ty teteke vaho vilie’e; ambolea’e tanem-bahe ami’ty vokam-pità’e.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Midian-kafatrarañe, naho ampaozare’e o sira’eo.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Oni’e te soa o balibalie’eo, tsy mikipe haleñe i failo’ey.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
An-dravem-pità’e ty fañareta’e, le tana’e an-delam-pità’e ty antsòli’e.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Velare’e amo rarakeo ty sira’e, vaho ahiti’e amo mavomavoo o fita’eo.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Tsy hembaña’e i fanalay amo keleia’eo; fa songa misiki-mañabasà o ana’eo.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Anjaira’e saroñe ty vata’e, hene leny naho malòmavo o siki’eo.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Fohiñe an-dalam-bey eo ty vali’e, ie mitrao-piambesatse amo androanavi’ i taneio.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Mitenoñe lamba leny re vaho aleta’e, tolora’e sokotry o mpanao takinakeo.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Haozarañe naho havantañañe ro fisiki’e, itohafa’e ty ho avy.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Sokafe’e an-kihitse ty falie’e, le fañòham-patarihañe ty am-pivimbi’e eo.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Halahalae’e soa o satan-keleia’eo, vaho tsy kamae’e ty mofon-kavotroañe.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Miongake o ana’eo mañandriañ’ aze, naho mandrenge aze i valie’ey.
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
Maro ty ampela manao soa, fe fonga ilikoara’o.
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Mpamañahy ty hasoa vintañe, kòake ty hamotramotràñe, fe rengèñe ty rakemba mañeveñe am’ Iehovà.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Atoloro aze ty havokaram-pità’e! le handrenge aze an-dalam-bey eo o sata’eo.