< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Berikut ini adalah nasihat yang diajarkan kepada Raja Lemuel oleh ibunya:
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Oh anakku, anak kandungku, anak yang aku janjikan kepada TUHAN untuk menjadi pelayan-Nya. Dengarkanlah baik-baik nasihatku.
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Jangan menghabis-habiskan kekayaan dan segala perhatianmu untuk menambah selir-selirmu, sebab banyak raja telah hancur karena hal itu.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
Hai Lemuel, sebagai raja, tidak pantas bagimu bermabuk-mabukan dengan minum anggur atau minuman keras yang lain, bahkan menginginkannya pun tidaklah patut.
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Karena bila engkau mabuk, engkau akan melupakan undang-undang negara dan menginjak-injak hak rakyat biasa.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Minuman keras hanya cocok bagi mereka yang sedang sekarat dan orang-orang yang merana.
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Biarlah mereka minum untuk melupakan kemiskinannya dan tak lagi mengingat-ingat masalahnya.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Sedangkan engkau, engkau harus bersuara nyaring bagi mereka yang tak berdaya dan perlu pelindung.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Gunakanlah posisimu untuk membuat keputusan yang adil dan membela hak orang yang miskin dan tertindas.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Sungguh beruntung apabila seorang lelaki mendapat istri yang cakap. Sungguh, wanita itu jauh lebih berharga daripada permata.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
Dia bisa dipercaya oleh suaminya, dan sang suami tak akan kekurangan untung.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Sepanjang hidup, dia mengusahakan yang baik bagi suaminya dan tak pernah merugikannya.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Dengan rajin dia mencari wol dan rami lalu membuat dua macam benang.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Istri yang cakap bagaikan kapal-kapal pedagang yang mendatangkan makanan dari mana pun.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Dia bangun sebelum matahari terbit untuk menyiapkan makanan bagi keluarganya, dan mengatur pekerjaan setiap budak perempuannya.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Dia mengatur rencana yang matang, dan dengan penghasilannya dari usaha-usaha yang lain dia membeli tanah lalu menanam kebun anggur.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Dia bekerja dengan cekatan, gesit, dan tangkas.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Istri yang cakap tahu bagaimana menghasilkan keuntungan dari pekerjaannya. Dia bekerja tekun sampai larut malam.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Dia mampu menggunakan alat pemintal benang, dan jari-jarinya menggulung dengan rapi.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Dia mau merangkul orang miskin dan mengulurkan tangan bagi yang membutuhkan.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Dia sudah menyiapkan baju hangat yang indah untuk seluruh keluarganya, sehingga tidak kuatir mereka kedinginan saat musim salju.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Dia mempercantik rumahnya dengan tirai dan berbagai hiasan kain yang dia buat sendiri. Semua pakaiannya indah dan berkualitas tinggi.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Suaminya dihormati masyarakat, terutama ketika duduk bersama para pemimpin di tempat pertemuan.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Sang istri membuat pakaian dan ikat pinggang dari linen untuk dijual kepada para pedagang.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Dia perempuan yang kuat dan dihormati semua orang. Dia bergembira karena tak cemas akan hari depan.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Ucapannya selalu bijaksana, memancarkan pengajaran dan kasih sayang.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Dia memperhatikan keadaan rumah tangganya dengan cermat dan tak pernah diam bermalas-malasan.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Anak-anaknya menghormati serta memujinya. Juga suaminya memuji dia, katanya,
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
“Wanita yang cakap ada banyak, tetapi engkau jauh melebihi mereka semua.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Penampilan dapat menipu, dan kecantikan akan hilang. Tetapi wanita yang takut akan TUHAN sungguh terpuji.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Balaslah segala hal baik yang sudah dilakukannya. Hasil pekerjaannya akan mengharumkan namanya di depan umum di kotanya.

< Miyambo 31 >