< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Dies sind die Worte des Königs Lamuel, die Lehre, die ihn seine Mutter lehrte.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Ach mein Auserwählter, ach du Sohn meines Leibes, ach mein gewünschter Sohn,
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
laß nicht den Weibern deine Kraft und gehe die Wege nicht, darin sich die Könige verderben!
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
O, nicht den Königen, Lamuel, nicht den Königen ziemt es, Wein zu trinken, noch den Fürsten starkes Getränk!
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Sie möchten trinken und der Rechte vergessen und verändern die Sache aller elenden Leute.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Gebt starkes Getränk denen, die am Umkommen sind, und den Wein den betrübten Seelen,
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
daß sie trinken und ihres Elends vergessen und ihres Unglücks nicht mehr gedenken.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Tue deinen Mund auf für die Stummen und für die Sache aller, die verlassen sind.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Tue deinen Mund auf und richte recht und räche den Elenden und Armen.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Wem ein tugendsam Weib beschert ist, die ist viel edler denn die köstlichsten Perlen.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
Ihres Mannes Herz darf sich auf sie verlassen, und Nahrung wird ihm nicht mangeln.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Sie tut ihm Liebes und kein Leides ihr Leben lang.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Sie geht mit Wolle und Flachs um und arbeitet gern mit ihren Händen.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Sie ist wie ein Kaufmannsschiff, das seine Nahrung von ferne bringt.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Sie steht vor Tages auf und gibt Speise ihrem Hause und Essen ihren Dirnen.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Sie denkt nach einem Acker und kauft ihn und pflanzt einen Weinberg von den Früchten ihrer Hände.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Sie gürtet ihre Lenden mit Kraft und stärkt ihre Arme.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Sie merkt, wie ihr Handel Frommen bringt; ihre Leuchte verlischt des Nachts nicht.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Sie streckt ihre Hand nach dem Rocken, und ihre Finger fassen die Spindel.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Sie breitet ihre Hände aus zu dem Armen und reicht ihre Hand dem Dürftigen.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Sie fürchtet für ihr Haus nicht den Schnee; denn ihr ganzes Haus hat zwiefache Kleider.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Sie macht sich selbst Decken; feine Leinwand und Purpur ist ihr Kleid.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Ihr Mann ist bekannt in den Toren, wenn er sitzt bei den Ältesten des Landes.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Sie macht einen Rock und verkauft ihn; einen Gürtel gibt sie dem Krämer.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Kraft und Schöne sind ihr Gewand, und sie lacht des kommenden Tages.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Sie tut ihren Mund auf mit Weisheit, und auf ihrer Zunge ist holdselige Lehre.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Sie schaut, wie es in ihrem Hause zugeht, und ißt ihr Brot nicht mit Faulheit.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Ihre Söhne stehen auf und preisen sie selig; ihr Mann lobt sie:
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
“Viele Töchter halten sich tugendsam; du aber übertriffst sie alle.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Lieblich und schön sein ist nichts; ein Weib, das den HERRN fürchtet, soll man loben.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Sie wird gerühmt werden von den Früchten ihrer Hände, und ihre Werke werden sie loben in den Toren.

< Miyambo 31 >