< Miyambo 31 >
1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Paroles du roi Lemouel. Leçon solennelle que lui inculqua sa mère.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
"Ah! mon fils! Ah! enfant de mes entrailles! Ah! fils que j’ai appelé de mes vœux!
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Ne prodigue paso ta vigueur aux femmes, ne livre pas tes destinées à celles qui perdent les rois.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
Ce n’est pas aux rois, ô Lemouel, ce n’est pas aux rois qu’il sied de boire du vin, ni aux princes de s’adonner aux liqueurs fortes;
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
de peur qu’en buvant, ils n’oublient les lois et ne méconnaissent le droit de toutes les victimes de la misère.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Donnez des liqueurs fortes aux malheureux, du vin à ceux qui ont l’amertume au cœur.
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Qu’ils boivent, et qu’ils oublient leur misère; qu’ils perdent le souvenir de leur chagrin!
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Ouvre la bouche en faveur du muet, pour la défense de tous les vaincus du sort.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Ouvre la bouche pour juger avec équité et faire droit au pauvre et à l’indigent.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Heureux qui a rencontré une femme vaillante! Elle est infiniment plus précieuse que les perles.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
En elle le cœur de son époux a toute confiance; aussi les ressources ne lui font-elles pas défaut.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Tous les jours de sa vie, elle travaille à son bonheur: jamais elle ne lui cause de peine.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Elle se procure de la laine et du lin et accomplit sa besogne d’une main diligente.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Pareille aux vaisseaux marchands, elle amène de loin ses provisions.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Il fait encore nuit qu’elle est déjà debout, distribuant des vivres à sa maison, des rations à ses servantes.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Elle jette son dévolu sur un champ et l’acquiert; avec le produit de son travail elle plante un vignoble.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Elle ceint de force ses reins et arme ses bras de vigueur.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Elle s’assure que ses affaires sont prospères; sa lampe ne s’éteint pas la nuit.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Ses mains saisissent le rouet, ses doigts manient le fuseau.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Elle ouvre sa main au pauvre et tend le bras au nécessiteux.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Elle ne redoute point la neige pour sa maison, car tous ses gens sont couverts de riches étoffes.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Elle se brode des tapis. Lin fin et pourpre forment ses vêtements.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Son époux est considéré aux Portes, quand il siège avec les anciens du pays.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Elle confectionne des tissus, qu’elle vend, et des ceintures, qu’elle cède au marchand.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Parée de force et de dignité, elle pense en souriant à l’avenir.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Elle ouvre la bouche avec sagesse, et des leçons empreintes de bonté sont sur ses lèvres.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Elle dirige avec vigilance la marche de sa maison, et jamais ne mange le pain de l’oisiveté.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Ses fils se lèvent pour la proclamer heureuse, son époux pour faire son éloge:
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
"Bien des femmes se sont montrées vaillantestu leur es supérieure à toutes!"
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Mensonge que la grâce! Vanité que la beauté! La femme qui craint l’Eternel est seule digne de louanges.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Rendez-lui hommage pour le fruit de ses mains, et qu’aux Portes ses œuvres disent son éloge!