< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
The words of King Lemuel—the revelation which his mother taught him:
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
“Oh, my son! Oh, son of my womb! Oh, son of my vows!
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Don’t give your strength to women, nor your ways to that which destroys kings.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
It is not for kings, Lemuel, it is not for kings to drink wine, nor for princes to say, ‘Where is strong drink?’
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
lest they drink, and forget the law, and pervert the justice due to anyone who is afflicted.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Give strong drink to him who is ready to perish, and wine to the bitter in soul.
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Let him drink, and forget his poverty, and remember his misery no more.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Open your mouth for the mute, in the cause of all who are left desolate.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Open your mouth, judge righteously, and serve justice to the poor and needy.”
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Who can find a worthy woman? For her value is far above rubies.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
The heart of her husband trusts in her. He shall have no lack of gain.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
She does him good, and not harm, all the days of her life.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
She seeks wool and flax, and works eagerly with her hands.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
She is like the merchant ships. She brings her bread from afar.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
She rises also while it is yet night, gives food to her household, and portions for her servant girls.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
She considers a field, and buys it. With the fruit of her hands, she plants a vineyard.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
She arms her waist with strength, and makes her arms strong.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
She perceives that her merchandise is profitable. Her lamp doesn’t go out by night.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
She lays her hands to the distaff, and her hands hold the spindle.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
She opens her arms to the poor; yes, she extends her hands to the needy.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
She is not afraid of the snow for her household, for all her household are clothed with scarlet.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
She makes for herself carpets of tapestry. Her clothing is fine linen and purple.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Her husband is respected in the gates, when he sits among the elders of the land.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
She makes linen garments and sells them, and delivers sashes to the merchant.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Strength and dignity are her clothing. She laughs at the time to come.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
She opens her mouth with wisdom. Kind instruction is on her tongue.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
She looks well to the ways of her household, and doesn’t eat the bread of idleness.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Her children rise up and call her blessed. Her husband also praises her:
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
“Many women do noble things, but you excel them all.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Charm is deceitful, and beauty is vain; but a woman who fears the LORD, she shall be praised.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Give her of the fruit of her hands! Let her works praise her in the gates!

< Miyambo 31 >