< Miyambo 31 >
1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
The words given to King Lemuel; the prophecy which his mother taught him.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
What, O my son! and what, O son of my womb! Yea, what, O son of my vows! [[shall I say to thee?]]
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Give not thy strength to women, Nor thy ways to that which destroyeth kings!
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
It is not for kings, O Lemuel! It is not for kings to drink wine, Nor for princes to desire strong drink;
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Lest they drink, and forget the law, And pervert the rights of any of the afflicted.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Give strong drink to him who is ready to perish, And wine to him that hath a heavy heart;
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Let him drink and forget his poverty, And remember his misery no more!
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Open thy mouth for the dumb, In the cause of every orphan!
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Open thy mouth, judge righteously, And maintain the cause of the poor and needy!
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Who can find a capable woman? Her worth is far above pearls.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
The heart of her husband trusteth in her, And he is in no want of gain.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
She doeth him good, and not evil, All the days of her life.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
She seeketh wool and flax, And worketh willingly with her hands.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
She is like the merchants' ships; She bringeth her food from afar.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
She riseth while it is yet night, And giveth food to her family, And a task to her maidens.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
She layeth a plan for a field, and buyeth it; With the fruit of her hands she planteth a vineyard.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
She girdeth her loins with strength, And maketh strong her arms.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
She perceiveth how pleasant is her gain, And her lamp is not extinguished in the night.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
She putteth forth her hands to the distaff, And her hands take hold of the spindle.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
She spreadeth out her hand to the poor, Yea, she reacheth forth her hands to the needy.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
She hath no fear for her household on account of the snow, For all her household are clothed with crimson.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
She maketh for herself coverlets; Her clothing is of fine linen and purple.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Her husband is known in the gates, When he sitteth with the elders of the land.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
She maketh linen garments and selleth them, And delivereth girdles to the merchant.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Strength and honor are her clothing; And she laugheth at the days to come.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
She openeth her mouth with wisdom, And kind instruction is upon her tongue.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
She looketh well to the ways of her household, And eateth not the bread of idleness.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Her children rise up, and extol her; Her husband, and praiseth her, [[saving, ]]
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
“Many daughters have done, virtuously, But thou excellest them all.”
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Grace is deceitful, and beauty vain; But the woman that feareth the LORD, she shall be praised.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Give ye her of the fruit of her hands, And let her works praise her in the gates.