< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Slova proroctví Lemuele krále, kterýmž vyučovala jej matka jeho.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Co dím, synu můj, co, synu života mého? Co, řku, dím, synu slibů mých?
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Nedávej ženám síly své, ani cest svých těm, kteréž k zahynutí přivodí krále.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
Ne králům, ó Lemueli, ne králům náleží píti víno, a ne pánům žádost nápoje opojného,
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Aby pije, nezapomněl na ustanovení, a nezměnil pře všech lidí ssoužených.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Dejte nápoj opojný hynoucímu, a víno těm, kteříž jsou truchlivého ducha,
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Ať se napije, a zapomene na chudobu svou, a na trápení své nezpomíná více.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Otevři ústa svá za němého, v při všech oddaných k smrti,
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Otevři, řku, ústa svá, suď spravedlivě, a veď při chudého a nuzného.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Ženu statečnou kdo nalezne? Nebo daleko nad perly cena její.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
Dověřuje se jí srdce muže jejího; nebo tu kořistí nebude nedostatku.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Dobře činí jemu a ne zle, po všecky dny života svého.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Hledá pilně vlny a lnu, a dělá šťastně rukama svýma.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Jest podobná lodi kupecké, zdaleka přiváží pokrm svůj.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Kterážto velmi ráno vstávajíc, dává pokrm čeledi své, a podíl náležitý děvkám svým.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Rozsuzuje pole, a ujímá je; z výdělku rukou svých štěpuje i vinici.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Přepasuje silou bedra svá, a zsiluje ramena svá.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Zakouší, jak jest užitečné zaměstknání její; ani v noci nehasne svíce její.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Rukama svýma sahá k kuželi, a prsty svými drží vřeteno.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Ruku svou otvírá chudému, a ruce své vztahuje k nuznému.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Nebojí se za čeled svou v čas sněhu; nebo všecka čeled její obláčí se v roucho dvojnásobní.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Koberce dělá sobě z kmentu, a z zlatohlavu jest oděv její.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Patrný jest v branách manžel její, když sedá s staršími země.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Plátno drahé dělá, a prodává; též i pasy prodává kupci.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Síla a krása oděv její, nestará se o časy potomní.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Ústa svá otvírá k moudrosti, a naučení dobrotivosti v jazyku jejím.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Spatřuje obcování čeledi své, a chleba zahálky nejí.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Povstanouce synové její, blahoslaví ji; manžel její také chválí ji,
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
Říkaje: Mnohé ženy statečně sobě počínaly, ty pak převyšuješ je všecky.
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Oklamavatelná jest příjemnost a marná krása; žena, kteráž se bojí Hospodina, tať chválena bude.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Dejtež takové z ovoce rukou jejích, a nechať ji chválí v branách skutkové její.

< Miyambo 31 >