< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
Amazwi kaAguri indodana kaJake umMasa. Umuntu wathi kuIthiyeli, kuIthiyeli loUkhali:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Isibili, ngiyisithutha kulomuntu, kangilakuqedisisa komuntu.
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
Kangifundanga inhlakanipho, kangilwazi ulwazi lwabangcwele.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Ngubani owenyukela emazulwini njalo wehla? Ngubani oqoqe wafumbatha umoya ezandleni zakhe? Ngubani ogoqele amanzi esembathweni? Ngubani omise yonke imikhawulo yomhlaba? Lingubani ibizo lakhe, lebizo lendodana yakhe lingubani, uba usazi?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Lonke ilizwi likaNkulunkulu licwengekile; uyisihlangu kwabaphephela kuye.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
Ungengezeleli emazwini akhe, hlezi akukhuze, utholwe ungumqambimanga.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Zimbili izinto engizicele kuwe; ungangigodleli zona ngingakafi.
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Susa khatshana lami ize lamazwi amanga; ungangiphi ubuyanga loba inotho; ungiphe ukudla kwesabelo sami.
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
Hlezi ngisuthe, ngikuphike ngithi: Ngubani iNkosi? Kumbe hlezi ngibe ngumyanga, ngintshontshe, ngithathe ngeze ibizo likaNkulunkulu wami.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
Ungahlebi inceku enkosini yayo, hlezi ikuthuke, ube lecala.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
Kulesizukulwana esithuka uyise, esingabusisi unina;
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
isizukulwana esihlambulukileyo emehlweni aso, kodwa esingahlanjululwanga engcekezeni yaso;
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
isizukulwana omehlo aso aphakeme kangaka, lenkophe zaso ziphakanyisiwe;
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
isizukulwana omazinyo aso zinkemba, lesimazinyo aso omhlathi zingqamu, zokudla abayanga emhlabeni, labaswelayo ebantwini.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
Umkhaza ulamadodakazi amabili athi: Phana, phana; lezizontathu kazisuthi; ezine kazitsho ukuthi: Kwanele.
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
Ingcwaba, lesizalo esiyinyumba, umhlaba ongasuthi amanzi, lomlilo ongathi: Kwanele. (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
Ilihlo eliklolodela uyise, lelidelela ukulalela unina, amawabayi esihotsha azalikopola, labantwana bamanqe bazalidla.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
Lezizinto ezintathu ziyisimangaliso esikhulu kimi, yebo, ezine engingazaziyo:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
Indlela yokhozi emazulwini, indlela yenyoka edwaleni, indlela yomkhumbi enhliziyweni yolwandle, lendlela yejaha entombini.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
Injalo indlela yowesifazana oliwule; udla, esule umlomo wakhe, athi: Kangenzanga isiphambeko.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
Ngenxa yezinto ezintathu umhlaba uyazamazama, yebo, ngenxa yezine ongezithwale:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
Ngenxa yesigqili nxa sibusa, lesithutha nxa sisuthi ukudla,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
ngenxa yesaliwakazi nxa sendile, lencekukazi nxa iyindlalifa yenkosikazi yayo.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
Lezi ezine zingezincinyane zomhlaba, kanti zihlakaniphile zenziwe zihlakaniphe:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
Ubunyonyo buyisizwe esingelamandla, kanti bulungisa ukudla kwabo ehlobo.
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
Imbila ziyisizwe esingelamandla, kanti zimisa indlu yazo edwaleni.
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
Intethe kazilankosi, kanti zonke ziphuma zehlukene ngamaviyo.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
Umbankwa ubambelela ngezandla ezimbili, njalo usezigodlweni zenkosi.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
Lezi ezintathu zinyathela kuhle, yebo, ezine zihamba kuhle:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
Isilwane esilamandla phakathi kwenyamazana, esingeyikubuyela emuva ngenxa yobuso loba ngobukabani;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
inja ebhince okhalweni, kumbe impongo; lenkosi ileviyo lamabutho.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
Uba ube yisithutha ngokuziphakamisa, njalo uba ucebe okubi, beka isandla emlonyeni.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Ngoba ukuphehlwa kochago kuveza iphehla, lokucindezelwa kwempumulo kuveza igazi, lokucindezelwa kwentukuthelo kuveza ingxabano.

< Miyambo 30 >