< Miyambo 30 >
1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
Paroles d'Agur, fils de Jaké. Sentences que cet homme prononça pour Ithiel, pour Ithiel et Ucal.
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Certainement je suis le plus borné de tous les hommes; je n'ai pas l'intelligence d'un homme.
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
Je n'ai pas appris la sagesse; et je ne connais pas la science des saints.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Qui est monté aux cieux, ou qui en est descendu? Qui a assemblé le vent dans ses mains? Qui a serré les eaux dans sa robe? Qui a dressé toutes les bornes de la terre? Quel est son nom, et quel est le nom de son fils? Le sais-tu
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Toute la parole de Dieu est épurée; il est un bouclier pour ceux qui ont en lui leur refuge.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
N'ajoute rien à ses paroles, de peur qu'il ne te reprenne, et que tu ne sois trouvé menteur.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Je t'ai demandé deux choses; ne me les refuse pas avant que je meure.
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Éloigne de moi la vanité et la parole de mensonge. Ne me donne ni pauvreté ni richesses; nourris-moi du pain de mon ordinaire;
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
De peur que dans l'abondance je ne te renie, et que je ne dise: Qui est l'Éternel? De peur aussi que dans la pauvreté je ne dérobe, et que je ne prenne en vain le nom de mon Dieu.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
Ne calomnie pas le serviteur devant son maître, de peur qu'il ne te maudisse, et qu'il ne t'en arrive du mal.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
Il y a une espèce de gens qui maudit son père, et qui ne bénit point sa mère.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
Il y a une race de gens qui se croit pure, et qui, toutefois, n'est pas lavée de sa souillure.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
Il y a une race de gens dont les yeux sont hautains, et les paupières élevées.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
Il y a une race de gens dont les dents sont comme des épées, et dont les mâchoires sont des couteaux, pour dévorer les affligés de dessus la terre et les pauvres d'entre les hommes.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
La sangsue a deux filles, qui disent: Apporte, apporte! Il y a trois choses qui ne se rassasient point; il y en a même quatre qui ne disent point: C'est assez!
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol )
Le Sépulcre, la femme stérile, la terre qui n'est point rassasiée d'eau, et le feu, qui ne dit point: C'est assez. (Sheol )
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
Les corbeaux des torrents crèveront l'œil de celui qui se moque de son père et qui méprise l'enseignement de sa mère, et les petits de l'aigle le mangeront.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
Il y a trois choses que je ne comprends point, même quatre, que je ne connais point:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
La trace de l'aigle dans l'air, la trace du serpent sur un rocher, le chemin d'un navire au milieu de la mer, et la trace de l'homme chez la jeune fille.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
Telle est la conduite de la femme adultère: elle mange, et s'essuie la bouche; puis elle dit: Je n'ai point commis de mal.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
La terre tremble pour trois choses, même pour quatre, et elle ne les peut porter:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
Pour un serviteur qui règne; pour un insensé qui est rassasié de nourriture,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
Pour une femme dédaignée qui se marie; et pour une servante qui hérite de sa maîtresse.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
Il y a quatre choses, des plus petites de la terre, qui, toutefois, sont sages et avisées:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
Les fourmis qui sont un peuple faible, et qui néanmoins préparent leur nourriture pendant l'été.
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
Les lapins, qui sont un peuple qui n'est pas puissant, et, cependant, ils font leurs maisons dans les rochers;
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
Les sauterelles qui n'ont point de roi, et, cependant, elles vont toutes par bandes;
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
Le lézard qui se tient avec ses mains, et qui est dans les palais des rois.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
Il y en a trois qui marchent bien, même quatre qui ont une belle démarche:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
Le lion, le plus fort d'entre les animaux, qui ne recule point devant qui que ce soit;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
Le cheval, aux flancs bien harnachés, et le bouc; et le roi à qui personne ne peut résister.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
Si tu as agi follement, en t'élevant toi-même, si tu as de mauvaises pensées, mets ta main sur ta bouche.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Comme celui qui bat le lait, fait sortir le beurre, et comme celui qui presse le nez fait sortir le sang, ainsi celui qui provoque la colère, excite la querelle.