< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
Paroles d’Agur, fils de Jaké, l’oracle prononcé par cet homme à Ithiel, à Ithiel et à Ucal:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Certes, moi je suis plus stupide que personne, et je n’ai pas l’intelligence d’un homme;
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
et je n’ai pas appris la sagesse, ni ne possède la connaissance du Saint.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Qui est monté dans les cieux, et qui en est descendu? Qui a rassemblé le vent dans le creux de ses mains? Qui a serré les eaux dans un manteau? Qui a établi toutes les bornes de la terre? Quel est son nom, et quel est le nom de son fils, si tu le sais?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Toute parole de Dieu est affinée; il est un bouclier pour ceux qui s’attendent à lui.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
N’ajoute pas à ses paroles, de peur qu’il ne te reprenne, et que tu ne sois trouvé menteur.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Je te demanderai deux choses; ne me les refuse pas, avant que je meure:
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Éloigne de moi la vanité et la parole de mensonge; ne me donne ni pauvreté ni richesse; nourris-moi du pain qui m’est nécessaire,
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
de peur que je ne sois rassasié, et que je ne te renie et ne dise: Qui est l’Éternel? et de peur que je ne sois appauvri, et que je ne dérobe, et que je ne parjure le nom de mon Dieu.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
N’accuse pas un serviteur auprès de son maître, de peur qu’il ne te maudisse, et que tu n’en portes la peine.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
Il est une génération qui maudit son père et qui ne bénit pas sa mère,
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
une génération pure à ses propres yeux et qui n’est pas lavée de son ordure,
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
une génération, … que ses yeux sont hautains, et ses paupières élevées!
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
– une génération dont les dents sont des épées et les molaires des couteaux, pour dévorer les affligés de dessus la terre, et les nécessiteux d’entre les hommes.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
La sangsue a deux filles: Donne! donne! Il y a trois choses qui sont insatiables, quatre qui ne disent pas: C’est assez!…
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
le shéol, et la matrice stérile, la terre qui n’est pas rassasiée d’eau, et le feu, qui ne dit pas: C’est assez! (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
L’œil qui se moque d’un père et qui méprise l’obéissance envers la mère, les corbeaux du torrent le crèveront et les petits de l’aigle le dévoreront.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
Trois choses sont trop merveilleuses pour moi, et il en est quatre que je ne puis connaître:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
le chemin de l’aigle dans les cieux, le chemin du serpent sur le rocher, le chemin d’un navire au cœur de la mer, et le chemin de l’homme vers la jeune fille.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
Tel est le chemin de la femme adultère: elle mange et s’essuie la bouche, et dit: Je n’ai point commis d’iniquité.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
Sous trois choses la terre tremble, et sous quatre elle n’en peut plus:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
sous le serviteur quand il règne, et l’homme vil quand il est rassasié de pain;
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
sous la femme odieuse quand elle se marie, et la servante quand elle hérite de sa maîtresse.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
Il y a quatre choses petites sur la terre, qui sont sages entre les sages:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
les fourmis, peuple sans force, et qui préparent en été leurs vivres;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
les damans, peuple sans puissance, et qui ont placé leurs maisons dans le rocher;
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
les sauterelles n’ont point de roi, mais elles sortent toutes par bandes;
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
tu saisis le lézard avec les mains, et il est dans les palais des rois.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
Il y a trois choses qui ont une belle allure, et quatre qui ont une belle démarche:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
le lion, le fort parmi les bêtes, et qui ne se détourne devant qui que ce soit;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
le [coursier] qui a les reins ceints; ou le bouc; et le roi, contre qui personne ne peut se lever.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
Si tu as agi follement en t’élevant et si tu as pensé à mal, [mets] la main sur ta bouche;
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Car la pression du lait produit le beurre, et la pression du nez fait sortir le sang, et la pression de la colère excite la querelle.

< Miyambo 30 >