< Miyambo 30 >
1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
The words of Agur the son of Jakeh, even the prophecy: the man spoke unto Ithiel, even unto Ithiel and Ucal,
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
Surely I am more brutish than any man, and have not the understanding of a man.
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
I neither learned wisdom, nor have the knowledge of the holy.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Who has ascended up into heaven, or descended? who has gathered the wind in his fists? who has bound the waters in a garment? who has established all the ends of the earth? what is his name, and what is his son's name, if you can tell?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
Every word of God is pure: he is a shield unto them that put their trust in him.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
Add you not unto his words, lest he reprove you, and you be found a liar.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Two things have I required of you; deny me them not before I die:
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Remove far from me vanity and lies: give me neither poverty nor riches; feed me with food convenient for me:
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
Lest I be full, and deny you, and say, Who is the LORD? or lest I be poor, and steal, and take the name of my God in vain.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
Accuse not a servant unto his master, lest he curse you, and you be found guilty.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
There is a generation that curses their father, and does not bless their mother.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
There is a generation that are pure in their own eyes, and yet is not washed from their filthiness.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
There is a generation, O how lofty are their eyes! and their eyelids are lifted up.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
There is a generation, whose teeth are as swords, and their jaw teeth as knives, to devour the poor from off the earth, and the needy from among men.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
The horseleach has two daughters, crying, Give, give. There are three things that are never satisfied, yea, four things say not, It is enough:
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol )
The grave; and the barren womb; the earth that is not filled with water; and the fire that says not, It is enough. (Sheol )
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
The eye that mocks at his father, and despises to obey his mother, the ravens of the valley shall pick it out, and the young eagles shall eat it.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
There be three things which are too wonderful for me, yea, four which I know not:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
The way of an eagle in the air; the way of a serpent upon a rock; the way of a ship in the midst of the sea; and the way of a man with a maid.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
Such is the way of an adulterous woman; she eats, and wipes her mouth, and says, I have done no wickedness.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
For three things the earth is disquieted, and for four which it cannot bear:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
For a servant when he reigns; and a fool when he is filled with food;
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
For an abhorrent woman when she is married; and an handmaid that is heir to her mistress.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
There be four things which are little upon the earth, but they are exceeding wise:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
The ants are a people not strong, yet they prepare their food in the summer;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
The conies are but a feeble folk, yet make they their houses in the rocks;
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
The locusts have no king, yet go they forth all of them by bands;
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
The spider takes hold with her hands, and is in kings' palaces.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
There be three things which go well, yea, four are comely in going:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
A lion which is strongest among beasts, and turns not away for any;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
A greyhound; an he goat also; and a king, against whom there is no rising up.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
If you have done foolishly in lifting up yourself, or if you have thought evil, lay your hand upon your mouth.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Surely the churning of milk brings forth butter, and the wringing of the nose brings forth blood: so the forcing of wrath brings forth strife.