< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
瑪薩人雅刻之子阿古爾的格言,即他給依提耳、給依提耳和烏加耳的斷語:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
我比誰都愚蠢,沒有人的才智。
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
我從來沒有學得智慧,致能通曉聖者的知識。
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
誰曾上升過天而又降下﹖誰能將風收集在手中﹖誰能將水聚集在大衣內﹖誰為這大地立定了邊界﹖他叫什麼名字﹖其子姓甚名誰﹖你知道嗎﹖
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
天主的每一句話,都是經火精煉的;凡托庇於他的人,他必要作其護盾。
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
對他所說的話,不可加添什麼;免得他指責你,證明你在說謊。
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
我求你兩件事,在我未死以前,請不要拒絕我:
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
令虛偽和欺詐遠離我,貧乏或富裕勿賜與我,只供予我必需的食糧,
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
免得我吃飽了,背叛你說:「誰是上主﹖」或是過於貧乏,因而行竊,加辱我天主的名。
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
別在主人前,誹謗他的奴僕,怕他咒罵你,你就不免受罰。
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
有一種人,咒罵父親;自己母親,也不祝福。
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
有一種人,自視清高;自身污穢,卻不洗滌。
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
有一種人,眼睛傲慢,目空一切。
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
有一種人,牙如利劍,齒如快刀,地上弱小,人間貧民,吞食一空。
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
水蛭有兩個女兒,常說「給我! 給我! 」不知足的東西,共有三樣,總不說「夠了」的,共有四樣:
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
即陰府、荒胎、總飲不足水的地,和總不說「夠了」的火。 (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
誰嘲笑父親,或輕視年老的母親,願他的眼睛,被谷中的烏鴉啄去,為小鷹所食。
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
令我稱奇的事,共有三樣,連我不明瞭的,共有四樣:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
即鷹在天空飛翔的道,蛇在岩石爬行的道,船在海中航行的道,以及男女交合之道。
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
淫婦的作風是這樣:她吃了後,抹抹口說:「我並沒有為非作歹。」
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
使地戰慄的事,共有三樣,連不可容忍的,共有四樣:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
即奴隸為王,愚人飽食,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
醜女出嫁,婢女當家。
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
地上的小動物中,有四種極其聰明:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
螞蟻是無力的一群,卻在夏日儲備食糧;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
岩貍是無能的一群,卻在岩石中築巢穴;
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
蝗虫雖然沒有君王,卻知一齊列隊出發;
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
壁虎能用手來捕捉,卻經常出入於皇宮。
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
舉止昂然之物,共有三樣,連威儀赫赫的,共有四樣:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
即獸中稱雄的獅子,面臨一切從不退縮;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
獨步雞群中的雄雞,開頭領隊的公山羊,和檢閱人民的君王。
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
你一時糊塗,高舉了自己,當你反省時,應以手掩口;
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
因為攪動乳汁,可出奶油;用力扭鼻,可流鮮血;激起憤怒,必生爭端。

< Miyambo 30 >