< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Mwanangu, usisahau mafundisho yangu, bali zitunze amri zangu moyoni mwako,
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
kwa kuwa zitakuongezea miaka mingi ya maisha yako na kukuletea mafanikio.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Usiache kamwe upendo na uaminifu vitengane nawe; vifunge shingoni mwako, viandike katika ubao wa moyo wako.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Ndipo utapata kibali na jina zuri mbele za Mungu na mwanadamu.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Mtumaini Bwana kwa moyo wako wote wala usizitegemee akili zako mwenyewe;
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
katika njia zako zote mkiri yeye, naye atayanyoosha mapito yako.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Usiwe mwenye hekima machoni pako mwenyewe; mche Bwana ukajiepushe na uovu.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Hii itakuletea afya mwilini mwako, na mafuta kwenye mifupa yako.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Mheshimu Bwana kwa mali zako na kwa malimbuko ya mazao yako yote;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
ndipo ghala zako zitakapojaa hadi kufurika, viriba vyako vitafurika kwa mvinyo mpya.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Mwanangu, usiidharau adhabu ya Bwana na usichukie kukaripiwa naye,
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
kwa sababu Bwana huwaadibisha wale awapendao, kama vile baba afanyavyo kwa mwana apendezwaye naye.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Heri mtu yule aonaye hekima, mtu yule apataye ufahamu,
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
kwa maana hekima ana faida kuliko fedha na mapato yake ni bora kuliko ya dhahabu safi.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Hekima ana thamani kuliko marijani; hakuna chochote unachokitamani kinachoweza kulinganishwa naye.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Maisha marefu yako katika mkono wake wa kuume; katika mkono wake wa kushoto kuna utajiri na heshima.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Njia zake zinapendeza, mapito yake yote ni amani.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Yeye ni mti wa uzima kwa wale wanaomkumbatia; wale wamshikao watabarikiwa.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Kwa hekima Bwana aliiweka misingi ya dunia, kwa ufahamu aliziweka mbingu mahali pake;
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
kwa maarifa yake vilindi viligawanywa, nayo mawingu yanadondosha umande.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Mwanangu, hifadhi maamuzi mema na busara, usiache vitoke machoni pako;
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
ndipo vitakapokuwa uzima nafsini mwako na pambo la neema shingoni mwako.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Kisha utaenda katika njia yako salama, wala mguu wako hautajikwaa;
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
ulalapo, hautaogopa; ulalapo usingizi wako utakuwa mtamu.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Usiogope maafa ya ghafula au maangamizi yanayowapata waovu,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
kwa kuwa Bwana atakuwa tumaini lako na kuepusha mguu wako kunaswa katika mtego.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Usizuie wema kwa wale wanaostahili ikiwa katika uwezo wako kutenda.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Usimwambie jirani yako, “Njoo baadaye, nitakupa kesho”: wakati wewe unacho kitu kile karibu nawe.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Usifanye hila ya kumdhuru jirani yako, ambaye anaishi karibu na wewe akikuamini.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Usimshtaki mtu bila sababu, wakati hajakutenda dhara lolote.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Usimwonee wivu mtu mwenye jeuri wala kuchagua njia yake iwayo yote,
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
kwa kuwa Bwana humchukia mtu mpotovu, lakini siri yake iko kwa mwenye haki.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Laana ya Bwana i juu ya nyumba ya mwovu, lakini yeye huibariki nyumba ya mwenye haki.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Huwadhihaki wale wanaodhihaki, lakini huwapa neema wale wanyenyekevu.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Wenye hekima hurithi heshima, bali huwaaibisha wapumbavu.

< Miyambo 3 >