< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Hijo mío, no olvides mis enseñanzas, Y tu corazón guarde mis mandamientos.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Porque largura de días, años de vida Y paz te aumentarán.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Nunca se aparten de ti la misericordia y la verdad. Átalas a tu cuello. Escríbelas en la tabla de tu corazón,
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Y hallarás gracia y buena opinión Ante los ojos de ʼElohim y del hombre.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confía en Yavé con todo tu corazón, Y no te apoyes en tu propia inteligencia.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Reconócelo en todos tus caminos, Y Él enderezará tus sendas.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
No seas sabio en tu propia opinión. Teme a Yavé Y apártate del mal,
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Porque será medicina a tu ombligo Y tuétano a tus huesos.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honra a Yavé con tus bienes Y con las primicias de todos tus frutos.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Tus graneros se henchirán de abundancia, Y tus lagares rebosarán de mosto.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Hijo mío, no menosprecies el castigo de Yavé, Ni te fatigues de su corrección.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Porque Yavé disciplina al que ama, Como el padre al hijo en quien se complace.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Inmensamente feliz el hombre que halla sabiduría Y el que obtiene la inteligencia.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Porque su provecho es mayor que el de la plata, Y su resultado es mejor que el oro fino.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Es más preciosa que las perlas, Nada de lo que desees podrá compararse con ella.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Abundancia de días hay en su mano derecha, Y en su izquierda, riquezas y honra.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Sus caminos son agradables, Y en todas sus sendas hay paz.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Es árbol de vida a los que echan mano a ella, Y los que la retienen son inmensamente felices.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Yavé fundó la tierra con sabiduría Y con entendimiento afirmó los cielos.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Con su conocimiento fueron divididos los océanos Y las nubes destilan rocío.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Hijo mío, no se aparten estas cosas de tus ojos. Guarda la sabiduría y la discreción,
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Y serán vida a tu alma y gracia a tu cuello.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Entonces andarás con seguridad en tu camino Y tu pie no tropezará.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Cuando te acuestas, no tendrás temor. Te acostarás, Y tu sueño será dulce.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
No temerás el pavor repentino, Ni cuando llega el ataque de los perversos,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Porque Yavé será tu Confianza. Él guardará tu pie de caer en la trampa.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
No retengas el bien a quien es debido, Cuando tienes el poder para hacerlo.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
No digas a tu prójimo: Anda y vuelve, mañana te lo daré, Cuando tienes contigo qué darle.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
No trames el mal contra el prójimo Que habita confiado junto a ti.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
No tengas pleito con alguno sin causa, Si no te hizo agravio.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
No envidies al hombre violento, Ni escojas alguno de sus caminos,
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Porque Yavé aborrece al perverso. Su íntima comunión es con los rectos.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
La maldición de Yavé está sobre la casa del impío, Pero bendice la morada de los justos.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Ciertamente Él se burla de los que se burlan Y da gracia a los humildes.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Los sabios heredarán honra, Pero los necios cargarán la afrenta.

< Miyambo 3 >