< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Hijo mío, no olvides mis enseñanzas, pero que tu corazón guarde mis mandamientos,
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
porque te añadirán la duración de los días, años de vida, y la paz.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
No dejes que la bondad y la verdad te abandonen. Átalos alrededor de tu cuello. Escríbelos en la tabla de tu corazón.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Así encontrarás el favor, y buen entendimiento ante Dios y los hombres.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confía en Yahvé con todo tu corazón, y no te apoyes en tu propio entendimiento.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Reconócelo en todos tus caminos, y él enderezará tus caminos.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
No seas sabio en tus propios ojos. Teme a Yahvé y apártate del mal.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Será salud para tu cuerpo, y alimento para tus huesos.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honra a Yahvé con tu sustancia, con las primicias de todo su incremento;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
para que tus graneros se llenen de abundancia, y sus cubas rebosarán de vino nuevo.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Hijo mío, no desprecies la disciplina de Yahvé, ni te canses de su corrección;
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
porque al que ama Yahvé, lo corrige, como un padre reprende al hijo en el que se deleita.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Feliz es el hombre que encuentra la sabiduría, el hombre que consigue la comprensión.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Para ella es mejor la ganancia que la obtención de plata, y su retorno es mejor que el oro fino.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Ella es más preciosa que los rubíes. Ninguna de las cosas que puedes desear se puede comparar con ella.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
La duración de los días está en su mano derecha. En su mano izquierda hay riquezas y honor.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Sus caminos son caminos de placer. Todos sus caminos son la paz.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Ella es un árbol de vida para los que se aferran a ella. Feliz es todo aquel que la retiene.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Por la sabiduría, Yahvé fundó la tierra. Mediante el entendimiento, estableció los cielos.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Por su conocimiento, las profundidades se rompieron, y los cielos dejan caer el rocío.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Hijo mío, que no se aparten de tus ojos. Mantén la sensatez y la discreción,
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
así serán la vida de tu alma, y gracia para tu cuello.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Entonces, seguirás tu camino con seguridad. Tu pie no tropezará.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Cuando te acuestes, no tendrás miedo. Sí, te acostarás y tu sueño será dulce.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
No tengas miedo del miedo repentino, ni de la desolación de los malvados, cuando llegue;
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
porque Yahvé será tu confianza, y evitará que te cojan el pie.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
No niegues el bien a quien se lo merece, cuando está en el poder de tu mano hacerlo.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
No digas a tu prójimo: “Vete y vuelve”; mañana te lo daré”. cuando lo tengas a tu lado.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
No trates de hacer el mal a tu prójimo, ya que habita con seguridad junto a ti.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
No te pelees con un hombre sin motivo, si no te ha hecho ningún daño.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
No envidies al hombre violento. No elijas ninguno de sus caminos.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Porque el perverso es una abominación para Yahvé, pero su amistad es con los rectos.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
La maldición de Yahvé está en la casa de los malvados, pero bendice la morada de los justos.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Seguramente se burla de los burlones, pero da gracia a los humildes.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Los sabios heredarán la gloria, pero la vergüenza será la promoción de los tontos.

< Miyambo 3 >