< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Hijo mío, no te olvides de mi ley; guarda en tu corazón mis preceptos,
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
porque te darán longevidad, (felices) años de vida y prosperidad.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
¡Que nunca la misericordia y la verdad se aparten de ti! Átalas a tu cuello, escríbelas en la tabla de tu corazón.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Así hallarás gracia y verdadera sabiduría a los ojos de Dios y a los ojos de los hombres.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confía en el Señor con todo tu corazón y no te apoyes en tu propia inteligencia.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
En todas tus empresas piensa en Él, y Él dirigirá tus caminos.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
No te creas sabio a tus ojos, teme a Dios, y huye del mal;
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
será medicina para tu cuerpo, y refrigerio para tus huesos.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honra a Dios con tu hacienda, y con las primicias de todos tus frutos;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
con eso se llenará de abundancia tus graneros, y tus lagares rebosarán de mosto.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
No deseches, hijo mío, la corrección de Yahvé, ni tengas aversión cuando Él te reprenda.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Pues Yahvé castiga a aquel a quien ama, como un padre al hijo en quien se complace.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
¡Dichoso el hombre que halló la sabiduría, el varón que ha adquirido la inteligencia!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Mejor es su adquisición que la de la plata; y más preciosos que el oro son sus frutos.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Ella es más apreciable que las perlas; no hay cosa deseable que la iguale.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
En su diestra (trae) larga vida, en su siniestra riquezas y honores.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Sus caminos son caminos deliciosos, y llenas de paz todas sus sendas.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Es árbol de vida para los que echan mano de ella, y dichoso el que la tiene asida.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Por la sabiduría fundó Dios la tierra, y por la inteligencia estableció los cielos;
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
por su ciencia fueron abiertos los abismos; y destilan las nubes rocío.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Hijo mío, no se aparten ellas de tus ojos; guarda la sabiduría y la prudencia;
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
pues serán vida para tu alma y adorno para tu cuello.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Así seguirás confiado tu camino, y no vacilará tu pie.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Te acostarás sin temor; y si te acuestas, tu sueño será dulce.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
No tendrás que temer repentinos espantos, ni los ataques de los impíos cuando te acometieren;
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
porque Yahvé estará a tu lado, y preservará tu pie de quedar preso.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
No niegues un beneficio al necesitado cuando esté a tu alcance el hacerlo.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
No digas a tu prójimo: “Vete y vuelve, mañana te daré”, estando en tu poder el (atenderlo).
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
No maquines ningún mal contra tu prójimo mientras él vive tranquilamente contigo.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Jamás pleitees con nadie sin motivo, si no te ha hecho mal.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
No envidies al hombre violento, ni sigas sus senderos.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Porque Yahvé detesta al perverso, pero tiene trato íntimo con los justos.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Sobre la casa del malvado pesa la maldición de Yahvé, el cual bendice la morada del justo.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Se burla de los burladores, y da su gracia a los humildes.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
La gloria es la herencia de los sabios, en tanto que los necios se acarrean ignominia.

< Miyambo 3 >