< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Фиуле, ну уйта ынвэцэтуриле меле ши пэстрязэ ын инима та сфатуриле меле!
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Кэч еле ыць вор лунӂи зилеле ши аний веций тале ши-ць вор адуче мултэ паче.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Сэ ну те пэрэсяскэ бунэтатя ши крединчошия: лягэ-ци-ле ла гыт, скрие-ле пе тэблица инимий тале!
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Ши, астфел, вей кэпэта тречере ши минте сэнэтоасэ ынаинтя луй Думнезеу ши ынаинтя оаменилор.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Ынкреде-те ын Домнул дин тоатэ инима та ши ну те бизуи пе ынцелепчуня та!
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Рекуноаште-Л ын тоате кэиле тале, ши Ел ыць ва нетези кэрэриле.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ну те сокоти сингур ынцелепт; теме-те де Домнул ши абате-те де ла рэу!
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Ачаста ва адуче сэнэтате трупулуй тэу ши рэкорире оаселор тале.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Чинстеште пе Домнул ку авериле тале ши ку челе динтый роаде дин тот венитул тэу,
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
кэч атунч грынареле ыць вор фи плине де белшуг ши тяскуриле тале вор ӂеме де муст.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Фиуле, ну диспрецуи мустраря Домнулуй ши ну те мыхни де педепселе Луй!
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Кэч Домнул мустрэ пе чине юбеште, ка ун пэринте пе копилул пе каре-л юбеште!
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Фериче де омул каре гэсеште ынцелепчуня ши де омул каре капэтэ причепере!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Кэч кыштигул пе каре-л адуче еа есте май бун декыт ал арӂинтулуй, ши венитул адус де еа есте май де прец декыт аурул;
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
еа есте май де прец декыт мэргэритареле ши тоате комориле тале ну се пот асемуи ку еа.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Ын дряпта ей есте о вяцэ лунгэ; ын стынга ей, богэцие ши славэ.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Кэиле ей сунт ниште кэй плэкуте ши тоате кэрэриле ей сунт ниште кэрэрь пашниче.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Еа есте ун пом де вяцэ пентру чей че о апукэ, ши чей че о ау сунт феричиць.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Прин ынцелепчуне а ынтемеят Домнул пэмынтул ши прин причепере а ынтэрит Ел черуриле;
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
прин штиинца Луй с-ау дескис адынкуриле ши стрекоарэ норий роуа.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Фиуле, сэ ну се депэртезе ынвэцэтуриле ачестя де окий тэй: пэстрязэ ынцелепчуня ши кибзуинца,
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
кэч еле вор фи вяца суфлетулуй тэу ши подоаба гытулуй тэу!
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Атунч вей мерӂе ку ынкредере пе друмул тэу, ши пичорул ну ци се ва потикни.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Кынд те вей кулка, вей фи фэрэ тямэ, ши кынд вей дорми, сомнул ыць ва фи дулче.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Ну те теме нич де спаймэ нэпрасникэ, нич де о нэвэлире дин партя челор рэй,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
кэч Домнул ва фи нэдеждя та ши Ел ыць ва пэзи пичорул де кэдере.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Ну опри о бинефачере челуй че аре невое де еа, кынд поць с-о фачь.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Ну зиче апроапелуй тэу: „Ду-те ши вино ярэшь; ыць вой да мыне”, кынд ай де унде сэ дай!
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Ну гынди рэу ымпотрива апроапелуй тэу, кынд локуеште лиништит лынгэ тине!
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Ну те черта фэрэ причинэ ку чинева, кынд ну ць-а фэкут ничун рэу!
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Ну пизмуи пе омул асупритор ши ну алеӂе ничуна дин кэиле луй!
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Кэч Домнул урэште пе оамений стрикаць, дар есте приетен ку чей фэрэ приханэ.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Блестемул Домнулуй есте ын каса челуй рэу, дар локуинца челор неприхэниць о бинекувынтязэ.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Кынд аре а фаче ку чей батжокориторь, Ышь бате жок де ей, дар челор смериць ле дэ хар.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Ынцелепций вор моштени слава, дар партя челор небунь есте рушиня.

< Miyambo 3 >