< Miyambo 3 >
1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Filho meu, não te esqueças da minha lei, e o teu coração guarde os meus mandamentos.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Porque eles te acrescentarão longura de dias, e anos de vida e paz.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Não te desamparem a benignidade e a fidelidade: ata-as ao teu pescoço; escreve-as na táboa do teu coração.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
E acharás graça e bom entendimento aos olhos de Deus e dos homens.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confia no Senhor com todo o teu coração, e não te estribes no teu próprio entendimento.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Reconhece-o em todos os teus caminhos, e ele endireitará as tuas veredas.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Não sejas sábio a teus próprios olhos: teme ao Senhor e aparta-te do mal.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Isto será saúde para o teu umbigo, e regadura para os teus ossos.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honra ao Senhor com a tua fazenda, e com as primícias de toda a tua renda.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
E se encherão os teus celeiros de fartura, e trasbordarão de mosto os teus lagares.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Filho meu, não rejeites a correção do Senhor, nem te enojes da sua repreensão.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Porque o Senhor repreende aquele a quem ama, assim como o pai ao filho a quem quer bem.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Bem-aventurado o homem que acha sabedoria, e o homem que produz inteligência.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Porque melhor é a sua mercadoria do que a mercadoria de prata, e a sua renda do que o ouro mais fino.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Mais preciosa é do que os rubins, e tudo o que mais podes desejar não se pode comparar a ela.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Longura de dias há na sua mão direita: na sua esquerda riquezas e honra.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Os caminhos dela são caminhos de delícias, e todas as suas veredas paz.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
É árvore da vida para os que dela pegam, e bem-aventurados são todos os que a reteem.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
O Senhor com sabedoria fundou a terra: preparou os céus com entendimento.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Pelo seu conhecimento se fenderam os abismos, e as nuvens destilam o orvalho.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Filho meu, não se apartem estes dos teus olhos: guarda a verdadeira sabedoria e o bom siso;
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Porque serão vida para a tua alma, e graça para o teu pescoço.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Então andarás com confiança pelo teu caminho, e não tropeçará o teu pé.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Quando te deitares, não temerás: mas te deitarás e o teu sono será suave.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Não temas o pavor repentino, nem a assolação dos ímpios quando vier.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Porque o Senhor será a tua esperança, e guardará os teus pés de os prenderem.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Não detenhas dos seus donos o bem, tendo na tua mão poder faze-lo.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Não digas ao teu próximo: vai, e torna, e amanhã to darei: tendo-o tu contigo.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Não maquines mal contra o teu próximo, pois habita contigo confiadamente.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Não contendas contra alguém sem razão, se te não tem feito mal.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Não tenhas inveja do homem violento, nem elejas algum de seus caminhos.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Porque o perverso é abominação ao Senhor, mas com os sinceros está o seu segredo.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
A maldição do Senhor habita na casa do ímpio, mas à habitação dos justos abençoará.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Certamente ele escarnecerá dos escarnecedores, mas dará graça aos mansos.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Os sábios herdarão honra, porém os loucos tomam sobre si confusão.