< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Son min, gløym ikkje læra mi! Lat hjarta varveitsla bodi mine!
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
For livetid lang og livs-år i mengd og velferd dei gjev deg i rikaste mål.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Lat ei kjærleik og truskap vika frå deg, men bitt deim um halsen på deg, skriv deim på di hjartetavla!
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Då vinn du ynde og fær godt vit for augo på Gud og menneskje.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Lit på Herren av heile ditt hjarta men set ikkje lit til ditt vit!
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Tenk på honom i all di ferd! So jamnar han dine vegar.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ver ikkje vis i eigne augo, ottast Herren og vik frå det vonde.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Det vert til helsebot for holdet ditt, og kveik for beini dine.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Æra Herren med eiga di og med fyrstegrøda av all di avling.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Då vert dine lødor rikleg fyllte, og safti renn yver i persorne dine.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Son min, ei du vanvyrde Herrens age, og ver ikkje leid for hans refsing!
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
For Herren agar den han elskar, som ein far med den son han hev kjær.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Sæl den mann som hev funne visdom, og den mann som vinn seg vit!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
For det er betre å kjøpa visdom enn sylv, og den vinning han gjev, er betre enn gull.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Dyrare er han enn perlor, av alle dine skattar er ingen som han.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Langt liv hev han i høgre handi, og i vinstre rikdom og æra.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Hans vegar er hugnads-vegar, og alle hans stigar er velferd.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Han er livsens tre for deim som grip han, og dei som held han fast, er sæle.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Med visdom hev Herren grunnfest jordi, med vit hev han laga himmelen.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Ved hans kunnskap fossa vatnet or djupi, og frå skyerne dryp det dogg.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Son min! Slepp ikkje augo av deim, tak vare på visdom og ettertanke!
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
So skal dei vera liv for sjæli di og prydnad um halsen din.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Då vandrar du trygt din veg og støyter ikkje din fot.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Når du legg deg, so kvekk du’kje upp, men du ligg og søv so godt.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Du skal ikkje ottast for bråstøkk, eller uver som yver ugudlege kjem.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
For Herren skal vera di tiltru, og han skal vara din fot frå snara.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Haldt ei burte det gode frå deim som treng det, når det stend i di magt å gjeva det!
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Seg ikkje til grannen din: «Gakk og kom att! Eg skal gjeva deg i morgon» - når du hev det no!
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Tenk ikkje på vondt mot grannen din, når han bur trygt hjå deg!
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Trætta ikkje med nokon utan grunn, når han ei hev gjort deg vondt!
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Ovunda ikkje ein valdsmann, og vel ikkje nokon av alle hans vegar!
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
For den falske er ei gruv for Herren, men med ærlege hev han umgang.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Herrens forbanning er i huset hjå den gudlause, men heimen åt rettferdige velsignar han.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Gjeld det spottarar, so spottar han, men dei audmjuke gjev han nåde.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Vismenner erver æra, men dårer ber med seg skam til løn.

< Miyambo 3 >