< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Fili mi, ne obliviscaris legis meae, et praecepta mea cor tuum custodiat.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
longitudinem enim dierum, et annos vitae, et pacem apponent tibi.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Misericordia, et veritas te non deserant, circumda eas gutturi tuo, et describe in tabulis cordis tui:
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
et invenies gratiam, et disciplinam bonam coram Deo et hominibus.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Habe fiduciam in Domino ex toto corde tuo, et ne innitaris prudentiae tuae.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
In omnibus viis tuis cogita illum, et ipse diriget gressus tuos.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ne sis sapiens apud temetipsum: time Deum, et recede a malo:
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
sanitas quippe erit umbilico tuo, et irrigatio ossium tuorum.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honora Dominum de tua substantia, et de primitiis omnium frugum tuarum da pauperibus:
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
et implebuntur horrea tua saturitate, et vino torcularia tua redundabunt.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Disciplinam Domini, fili mi, ne abiicias: nec deficias cum ab eo corriperis:
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
quem enim diligit Dominus, corripit: et quasi pater in filio complacet sibi.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Beatus homo, qui invenit sapientiam, et qui affluit prudentia:
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
melior est acquisitio eius negotiatione auri, et argenti primi et purissimi fructus eius:
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
pretiosior est cunctis opibus: et omnia, quae desiderantur, huic non valent comparari.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Longitudo dierum in dextera eius, et in sinistra illius divitiae, et gloria.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Viae eius viae pulchrae, et omnes semitae illius pacificae.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Lignum vitae est his, qui apprehenderint eam: et qui tenuerit eam, beatus.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Dominus sapientia fundavit terram, stabilivit caelos prudentia.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Sapientia illius eruperunt abyssi, et nubes rore concrescunt.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Fili mi, ne effluant haec ab oculis tuis: Custodi legem atque consilium:
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
et erit vita animae tuae, et gratia faucibus tuis.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
tunc ambulabis fiducialiter in via tua, et pes tuus non impinget:
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
si dormieris, non timebis: quiesces, et suavis erit somnus tuus.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
ne paveas repentino terrore, et irruentes tibi potentias impiorum.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Dominus enim erit in latere tuo, et custodiet pedem tuum ne capiaris.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Noli prohibere benefacere eum, qui potest: si vales, et ipse benefac:
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Ne dicas amico tuo: Vade, et revertere: cras dabo tibi: cum statim possis dare.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Ne moliaris amico tuo malum, cum ille in te habeat fiduciam.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Ne contendas adversus hominem frustra, cum ipse tibi nihil mali fecerit.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Ne aemuleris hominem iniustum, nec imiteris vias eius:
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
quia abominatio Domini est omnis illusor, et cum simplicibus sermocinatio eius.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Egestas a Domino in domo impii: habitacula autem iustorum benedicentur.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Ipse deludet illusores, et mansuetis dabit gratiam.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Gloriam sapientes possidebunt: stultorum exaltatio, ignominia.

< Miyambo 3 >