< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Anakku, janganlah melupakan ajaranku. Simpanlah segala perintahku di dalam hatimu
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
agar panjang umurmu dan tenteram hidupmu.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Hendaklah engkau senantiasa digerakkan oleh kebaikan hati dan kesetiaan. Jadikan keduanya seperti kalung pengingat pada lehermu. Ukirkanlah itu di dalam hatimu,
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
maka engkau akan dikasihi dan dihormati di hadapan Allah maupun manusia.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Percayalah kepada TUHAN dengan sepenuh hatimu dan jangan mengandalkan pemikiranmu sendiri.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Mintalah kehendak-Nya dalam setiap langkah hidupmu, maka Dia akan menuntunmu ke jalan yang benar.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Janganlah berpikir bahwa dirimu sudah bijaksana. Takutlah kepada TUHAN dan jauhilah yang jahat.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Itulah jamu yang akan membuat tubuhmu sehat dan selalu segar.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Pergunakanlah apa pun yang engkau miliki untuk menghormati TUHAN, dan persembahkanlah bagian terbaik dari segala penghasilanmu.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Maka oleh berkat TUHAN, gudang-gudangmu tidak akan cukup besar untuk memuat semua hasil panenmu, dan penampungan air anggurmu tidak akan cukup memuat hasil pemerasan buah anggurmu.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Anakku, janganlah menolak didikan TUHAN, dan jangan marah bila Dia menegurmu.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Karena TUHAN menegur orang yang Dia kasihi, seperti seorang ayah mendidik anak yang dikasihinya untuk memperbaiki kelakuannya.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Sungguh berbahagia bila engkau menyambut Sang Hikmat menjadi guru kehidupanmu! Darinyalah engkau akan menerima wawasan.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Sebab hasil pengajaran Sang Hikmat lebih berharga daripada perak maupun emas murni,
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
bahkan lebih bernilai daripada batu permata. Semua yang diinginkan manusia tak sebanding dengannya.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Hikmat itu membawakan bagimu umur panjang di tangan kanannya, juga kekayaan dan kehormatan di tangan kirinya.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Dia akan menuntunmu di jalan hidup yang menyenangkan dan penuh ketenangan.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Memiliki dia akan membuatmu panjang umur, seperti menemukan pohon kehidupan. Bila engkau tetap berpegang padanya, engkau akan sangat diberkati.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Dengan hikmat itulah TUHAN menciptakan langit dan bumi. Dengan perhitungan yang bijaksana Dia mengatur segala air dan hujan.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Jadi anakku, utamakanlah kebijaksanaan dan kematangan berpikir. Simpanlah keduanya baik-baik di dalam dirimu.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Dengan begitu, engkau akan berumur panjang dan beroleh nama baik.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Engkau pun akan hidup dengan aman tanpa tersandung bahaya kesalahan.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Maka engkau dapat tidur lelap, karena tiadalah resah dan gelisah.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Engkau tak perlu takut saat bencana tiba-tiba datang. Orang jahat akan dihantam, tetapi engkau tetap aman,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
sebab engkau bersandar kepada TUHAN. Dialah yang menjagamu dari perangkap musuhmu.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Waktu sesamamu memerlukan bantuan, janganlah berdiam diri. Bantulah dia bila engkau mampu.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Apa yang dapat engkau berikan hari ini, berikanlah tanpa menunda. Jangan katakan kepadanya, “Besok saja aku membantumu.”
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Jangan sekali-kali merencanakan kejahatan terhadap orang di sekitarmu, karena mereka merasa aman di dekatmu.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Jika sesamamu tidak bersalah terhadap engkau, jangan memulai pertengkaran dengannya.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Jangan iri hati kepada orang yang mendapat harta dengan kekerasan. Jangan meniru cara hidup mereka.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Sebab TUHAN membenci orang jahat, tetapi menjadi sahabat bagi orang jujur.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Seluruh isi rumah orang jahat berada di bawah kutukan TUHAN, tetapi rumah tangga orang benar diberkati-Nya.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
TUHAN memandang rendah orang yang menghina orang lain, tetapi bermurah hati kepada orang yang rendah hati.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Orang bijak akan mendapat kehormatan tanpa mencarinya, tetapi orang bebal akan bergelimang aib.

< Miyambo 3 >