< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Anakko, saanmo a liplipatan dagiti bilbilinko, ken tungpalem dagiti sursurok dita pusom,
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
ta inayonda kenka ti atiddog nga al-aldaw, ken tawtawen ti panagbiag, ken talna.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Saanmo nga ipalubos a panawannaka ti kinapudno ti tulag ken kinamatalek, maiyarig dagitoy iti kwintas nga igalutmo iti tengngedmo, isuratmo dagitoy dita pusom.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Iti kasta makasarakkanto iti pabor ken nasayaat a pakasaritaan iti imatang ti Dios ken tao.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Agtalekka kenni Yahweh iti amin a pusom ken saanka nga agtalek iti bukodmo a pannakaawat;
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
iti amin a dalanmo, bigbigem isuna ket palintegennanto dagiti pagnaam.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Saanmo nga ipagarup a masiribka; agbutengka kenni Yahweh ket tallikudam ti kinadakes.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Agbalinto daytoy a pannakapaimbag ti lasagmo ken pannakapapigsa ti bagim.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Dayawem ni Yahweh iti kinabaknangmo ken kadagiti umuna a bunga dagiti amin nga apitmo,
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
ket mapnonto dagiti kamaligmo ken aglupluppiasto dagiti burnaymo, a napno iti baro nga arak.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Anakko, saanmo a laisen ti panangdisiplina ni Yahweh ken saanmo a guraen ti panangtubngarna,
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
ta disdisiplinaen ni Yahweh dagiti ay-ayatenna, a kas iti panangdisiplina ti maysa nga ama iti anakna a makaay-ayo kenkuana.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Naragsak ti makasarak iti kinasirib, makagun-od met isuna iti pannakaawat.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Nasaysayaat ti magun-odmo iti kinasirib ngem iti magun-odmo iti pirak ken nasaysayaat ti magungguna iti kinasirib ngem iti balitok.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Napatpateg ti kinasirib ngem kadagiti alahas ken awan kadagiti tartarigagayam ti maiyasping kenkuana.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Adda iti makannawan nga imana dagiti al-aldaw; adda iti makannigid nga imana dagiti kinabaknang ken pammadayaw.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Dagiti wagasna ket wagwagas ti kinaimbag ken amin dagiti wagasna ket talna.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Isuna ket maiyarig a kayo ti biag kadagiti kumpet kenkuana, naragsak dagiti agtalinaed iti daytoy.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Babaen iti kinasirib ket inaramid ni Yahweh ti daga, babaen iti kinalaingna ket inkabilna dagiti adda iti langit.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Babaen iti pannakaammona ket naglukat dagiti yuyeng ken intinnag dagiti ulep ti linnaawda.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Anakko, salimetmetam ti naimbag a panangukom ken pannakaammo, ken saanmo nga isinsina ti panagkitam kadagitoy.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Agbalindanto a biag ti kararuam ken a kuwintas ti bendision nga isuotmo iti tengngedmo.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Ket magnakanto iti dalanmo a sitatalged ken saanto a maitibkol ti sakam;
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
inton agiddaka, saankanto nga agbuteng; inton agiddaka, mayatto ti pannaturogmo.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Saanka nga agbuteng iti inton adda kellaat a dumteng ti pagbutngan wenno panangdadael dagiti nadadangkes,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
ta addanto ni Yahweh iti abaymo ket saluadannanto ta sakam manipud iti pannakapalab-ogna.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Saanmo nga iyimot ti kinaimbag kadagiti maikari iti daytoy, no adda kabaelam a mangaramid iti daytoy.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Saanmo a kunaen iti kaarrubam, “Agsublikanto no bigat ket itedkonto kenka,” idinto nga addan kenka ti kuarta.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Saanka nga agpanggep a mangdangran iti kaarrubam— ti agnanaed iti asidegmo ken agtaltalek kenka.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Saanka a makirinikiar nga awan gapgapuna iti maysa a tao, idinto nga awan inaramidna kenka a dakes.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Saanka nga umapal iti naranggas a tao wenno mangpili iti aniaman kadagiti wagasna.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Ta ti ulbod a tao ket makarimon kenni Yahweh, ngem iyasidegna kenkuana dagiti nalinteg a tattao.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Ti lunod ni Yahweh ket adda iti balay dagiti nadangkes a tattao, ngem benbendisionanna ti pagtaengan dagiti nalinteg a tattao.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Lalaisenna dagiti mananglais, ngem kakaasianna dagiti napakumbaba a tattao.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Tawiden dagiti nasirib a tattao ti pammadayaw, ngem maibabainto dagiti maag.

< Miyambo 3 >