< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Mon fils, ne mets point en oubli mon enseignement, et que ton cœur garde mes commandements.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Car ils t'apporteront de longs jours, et des années de vie, et de prospérité.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Que la gratuité et la vérité ne t'abandonnent point: lie-les à ton cou, et écris-les sur la table de ton cœur;
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Et tu trouveras la grâce et le bon sens aux yeux de Dieu et des hommes.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confie-toi de tout ton cœur en l'Eternel, et ne t'appuie point sur ta prudence.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Considère-le en toutes tes voies, et il dirigera tes sentiers.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ne sois point sage à tes yeux; crains l'Eternel, et détourne-toi du mal.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Ce sera une médecine à ton nombril, et une humectation à tes os.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honore l'Eternel de ton bien, et des prémices de tout ton revenu.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Et tes greniers seront remplis d'abondance, et tes cuves rompront de moût.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Mon fils, ne rebute point l'instruction de l'Eternel, et ne te fâche point de ce qu'il te reprend.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Car l'Eternel reprend celui qu'il aime, même comme un père l'enfant auquel il prend plaisir.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Ô! que bienheureux est l'homme [qui] trouve la sagesse, et l'homme qui met en avant l'intelligence!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Car le trafic qu'on peut faire d'elle, est meilleur que le trafic de l'argent; et le revenu qu'on en peut avoir, est meilleur que le fin or.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Elle est plus précieuse que les perles, et toutes tes choses désirables ne la valent point.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Il y a de longs jours en sa main droite, des richesses et de la gloire en sa gauche.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Ses voies sont des voies agréables, et tous ses sentiers ne sont que prospérité.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Elle est l'arbre de vie à ceux qui l'embrassent; et tous ceux qui la tiennent sont rendus bienheureux.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
L'Eternel a fondé la terre par la sapience, et il a disposé les cieux par l'intelligence.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Les abîmes se débordent par sa science, et les nuées distillent la rosée.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Mon fils, qu'elles ne s'écartent point de devant tes yeux; garde la droite connaissance et la prudence.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Et elles seront la vie de ton âme, et l'ornement de ton cou.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Alors tu marcheras en assurance par ta voie, et ton pied ne bronchera point.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Si tu te couches, tu n'auras point de frayeur, et quand tu te seras couché ton sommeil sera doux.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Ne crains point la frayeur subite, ni la ruine des méchants, quand elle arrivera.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Car l'Eternel sera ton espérance, et il gardera ton pied d'être pris.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Ne retiens pas le bien de ceux à qui il appartient, encore qu'il fût en ta puissance de le faire.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Ne dis point à ton prochain: Va, et retourne, et je te le donnerai demain, quand tu l'as par-devers toi.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Ne machine point de mal contre ton prochain; vu qu'il habite en assurance avec toi.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
N'aie point de procès sans sujet avec aucun, à moins qu'il ne t'ait fait quelque tort.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Ne porte point d'envie à l'homme violent, et ne choisis aucune de ses voies.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Car celui qui va de travers est en abomination à l'Eternel; mais son secret est avec ceux qui sont justes.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
La malédiction de l'Eternel est dans la maison du méchant; mais il bénit la demeure des justes.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Certes il se moque des moqueurs, mais il fait grâce aux débonnaires.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Les sages hériteront la gloire; mais l'ignominie élève les fous.

< Miyambo 3 >