< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Mon fils, n’oublie pas mon enseignement, et que ton cœur garde mes commandements;
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
car ils t’ajouteront un prolongement de jours, et des années de vie, et la paix.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Que la bonté et la vérité ne t’abandonnent pas; lie-les à ton cou, écris-les sur la tablette de ton cœur,
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
et tu trouveras la faveur et la bonne sagesse aux yeux de Dieu et des hommes.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Confie-toi de tout ton cœur à l’Éternel, et ne t’appuie pas sur ton intelligence;
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
dans toutes tes voies connais-le, et il dirigera tes sentiers.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Ne sois pas sage à tes propres yeux; crains l’Éternel et éloigne-toi du mal:
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
ce sera la santé pour ton nombril, et un arrosement pour tes os.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honore l’Éternel de tes biens et des prémices de tout ton revenu;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
et tes greniers se rempliront d’abondance, et tes cuves regorgeront de moût.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Mon fils, ne méprise pas l’instruction de l’Éternel, et n’aie pas en aversion sa réprimande;
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
car celui que l’Éternel aime, il le discipline, comme un père le fils auquel il prend plaisir.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Bienheureux l’homme qui trouve la sagesse, et l’homme qui obtient l’intelligence!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
car son acquisition est meilleure que l’acquisition de l’argent, et son revenu [est meilleur] que l’or fin.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Elle est plus précieuse que les rubis, et aucune des choses auxquelles tu prends plaisir ne l’égale:
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
longueur de jours est dans sa droite, dans sa gauche richesse et honneur;
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
ses voies sont des voies agréables, et tous ses sentiers sont paix.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Elle est un arbre de vie pour ceux qui la saisissent; et qui la tient ferme est rendu bienheureux.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
L’Éternel a fondé la terre par la sagesse, il a établi les cieux par l’intelligence.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Par sa connaissance les abîmes se fendirent, et les nuées distillent la rosée.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Mon fils, que [ces choses] ne s’éloignent point de tes yeux: garde le sain conseil et la réflexion,
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
et ils seront la vie de ton âme et la grâce de ton cou.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Alors tu iras ton chemin en sécurité, et ton pied ne se heurtera point.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Si tu te couches tu n’auras point de crainte; mais tu te coucheras et ton sommeil sera doux.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Ne crains pas la frayeur subite, ni la ruine des méchants quand elle surviendra;
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
car l’Éternel sera ta confiance, et il gardera ton pied d’être pris.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Ne refuse pas le bien à celui à qui il est dû, quand il est au pouvoir de ta main de le faire.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Ne dis pas à ton prochain: Va et reviens, et je te le donnerai demain, quand tu as la chose par-devers toi.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Ne machine pas du mal contre ton prochain, puisqu’il habite en sécurité près de toi.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Ne conteste pas sans sujet avec un homme, s’il ne t’a pas fait de tort.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Ne porte pas envie à un homme violent, et ne choisis aucune de ses voies;
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Car l’Éternel a en abomination le pervers, et son secret est avec les hommes droits.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
La malédiction de l’Éternel est dans la maison du méchant, et il bénit l’habitation des justes.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Certes il se moque des moqueurs, et il donne la grâce aux débonnaires.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Les sages hériteront la gloire, mais la honte est l’élévation des sots.

< Miyambo 3 >