< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Mijn zoon! vergeet mijn wet niet, maar uw hart beware mijn geboden.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Want langheid van dagen, en jaren van leven, en vrede zullen zij u vermeerderen.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Dat de goedertierenheid en de trouw u niet verlaten; bind ze aan uw hals, schrijf zij op de tafel uws harten.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
En vind gunst en goed verstand, in de ogen Gods en der mensen.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Vertrouw op den HEERE met uw ganse hart, en steun op uw verstand niet.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Ken Hem in al uw wegen, en Hij zal uw paden recht maken.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Zijt niet wijs in uw ogen; vrees den HEERE, en wijk van het kwade.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Het zal een medicijn voor uw navel zijn, en een bevochtiging voor uw beenderen.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Vereer den HEERE van uw goed, en van de eerstelingen al uwer inkomsten;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Zo zullen uw schuren met overvloed vervuld worden, en uw perskuipen van most overlopen.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Mijn zoon! verwerp de tucht des HEEREN niet, en wees niet verdrietig over Zijn kastijding;
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Want de HEERE kastijdt dengene, dien Hij liefheeft, ja, gelijk een vader den zoon, in denwelken hij een welbehagen heeft.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Welgelukzalig is de mens, die wijsheid vindt, en de mens, die verstandigheid voortbrengt!
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Want haar koophandel is beter dan de koophandel van zilver, en haar inkomst dan het uitgegraven goud.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Zij is kostelijker dan robijnen; en al wat u lusten mag, is met haar niet te vergelijken.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Langheid der dagen is in haar rechterhand, in haar linkerhand rijkdom en eer.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Haar wegen zijn wegen der liefelijkheid, en al haar paden vrede.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Zij is een boom des levens dengenen, die ze aangrijpen, en elkeen, die ze vast houdt, wordt gelukzalig.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
De HEERE heeft de aarde door wijsheid gegrond, de hemelen door verstandigheid bereid.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Door Zijn wetenschap zijn de afgronden gekloofd, en de wolken druipen dauw.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Mijn zoon! laat ze niet afwijken van uw ogen; bewaar de bestendige wijsheid en bedachtzaamheid.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Want zij zullen het leven voor uw ziel zijn, en een aangenaamheid voor uw hals.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Dan zult gij uw weg zeker wandelen, en gij zult uw voet niet stoten.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Zo gij nederligt, zult gij niet schrikken; maar gij zult nederliggen en uw slaap zal zoet wezen.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Vrees niet voor haastigen schrik, noch voor de verwoesting der goddelozen, als zij komt.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Want de HEERE zal met uw hoop wezen, en Hij zal uw voet bewaren van gevangen te worden.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Onthoud het goed van zijn meesters niet, als het in het vermogen uwer hand is te doen.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Zeg niet tot uw naaste: Ga heen, en kom weder, en morgen zal ik geven, dewijl het bij u is.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Smeed geen kwaad tegen uw naaste, aangezien hij met vertrouwen bij u woont.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Twist met een mens niet zonder oorzaak, zo hij u geen kwaad gedaan heeft.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Zijt niet nijdig over een man des gewelds, en verkies geen van zijn wegen.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Want de afwijker is den HEERE een gruwel; maar Zijn verborgenheid is met den oprechte.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
De vloek des HEEREN is in het huis des goddelozen; maar de woning der rechtvaardigen zal Hij zegenen.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Zekerlijk, de spotters zal Hij bespotten, maar den zachtmoedigen zal Hij genade geven.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
De wijzen zullen eer beerven; maar elk een der zotten neemt schande op zich.

< Miyambo 3 >