< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Synu můj, na učení mé nezapomínej, ale přikázaní mých nechať ostříhá srdce tvé.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Dlouhosti zajisté dnů, i let života i pokoje přidadí tobě.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Milosrdenství a pravda nechť neopouštějí tě, přivaž je k hrdlu svému, napiš je na tabuli srdce svého,
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
A nalezneš milost a prospěch výborný před Bohem i lidmi.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Doufej v Hospodina celým srdcem svým, na rozumnost pak svou nezpoléhej.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Na všech cestách svých snažuj se jej poznávati, a onť spravovati bude stezky tvé.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Nebývej moudrý sám u sebe; boj se Hospodina, a odstup od zlého.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Toť bude zdraví životu tvému, a rozvlažení kostem tvým.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Cti Hospodina z statku svého, a z nejpřednějších věcí všech úrod svých,
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
A naplněny budou stodoly tvé hojností, a presové tvoji mstem oplývati budou.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Kázně Hospodinovy, synu můj, nezamítej, aniž sobě oškliv domlouvání jeho.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Nebo kohož miluje Hospodin, tresce, a to jako otec syna, jejž libuje.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Blahoslavený člověk nalézající moudrost, a člověk vynášející opatrnost.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Lépeť jest zajisté těžeti jí, nežli těžeti stříbrem, anobrž nad výborné zlato užitek její.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Dražší jest než drahé kamení, a všecky nejžádostivější věci tvé nevrovnají se jí.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Dlouhost dnů v pravici její, a v levici její bohatství a sláva.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Cesty její cesty utěšené, a všecky stezky její pokojné.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Stromem života jest těm, kteříž jí dosahují, a kteříž ji mají, blahoslavení jsou.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Hospodin moudrostí založil zemi, utvrdil nebesa opatrností.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Uměním jeho propasti protrhují se, a oblakové vydávají rosu.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Synu můj, nechť neodcházejí ty věci od očí tvých, ostříhej zdravého naučení a prozřetelnosti.
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
I budeť to životem duši tvé, a ozdobou hrdlu tvému.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Tehdy choditi budeš bezpečně cestou svou, a v nohu svou neurazíš se.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Když lehneš, nebudeš se strašiti, ale odpočívati budeš, a bude libý sen tvůj.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Nelekneš se strachu náhlého, ani zpuštění bezbožníků, když přijde.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Nebo Hospodin bude doufání tvé, a ostříhati bude nohy tvé, abys nebyl lapen.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Nezadržuj dobrodiní potřebujícím, když s to býti můžeš, abys je činil.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Neříkej bližnímu svému: Odejdi, potom navrať se, a zítrať dám, maje to u sebe.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Neukládej proti bližnímu svému zlého, kterýž s tebou dověrně bydlí.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Nevaď se s člověkem bez příčiny, jestližeť neučinil zlého.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Nechtěj záviděti muži dráči, aniž zvoluj které cesty jeho.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Nebo ohavností jest Hospodinu převrácenec, ale s upřímými tajemství jeho.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Zlořečení Hospodinovo jest v domě bezbožníka, ale příbytku spravedlivých žehná:
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Poněvadž posměvačům on se posmívá, pokorným pak dává milost.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Slávu moudří dědičně obdrží, ale blázny hubí pohanění.

< Miyambo 3 >