< Miyambo 3 >
1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Сине мой, не забравяй поуката ми, И сърцето ти нека пази заповедите ми,
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Защото дългоденствие, години от живот И мир ще ти притурят те.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Благост и вярност нека не те оставят; Вържи ги около шията си, Начертай ги на плочата на сърцето си.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Така ще намериш благоволение и добро име Пред Бога и човеците.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Уповавай на Господа от все сърце И не се облягай на своя разум.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Във всичките си пътища признавай Него, И Той ще оправя пътеките ти.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Не мисли себе си за мъдър; Бой се от Господа, и отклонявай се от зло;
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Това ще бъде здраве за тялото ти И влага за косите ти.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Почитай Господа от имота си И от първаците на всичкия доход.
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Така ще се изпълнят житниците ти с изобилие, И линовете ти ще се преливат с ново вино.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Сине мой, не презирай наказанието от Господа, И да ти не дотегва, когато Той те изобличава,
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Защото Господ изобличава оня, когото люби, Както и бащата сина, който му е мил.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Блажен оня човек, който е намерил мъдрост, И човек, който е придобил разум,
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Защото търговията с нея е по-износна от търговията със сребро, И печалбата от нея по-скъпа от чисто злато.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Тя е по-скъпа от безценни камъни И нищо, което би пожелал ти, не се сравнява с нея.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Дългоденствие е в десницата й, А в левицата й богатство и слава.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Пътищата й са пътища приятни, И всичките й пътеки мир.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Тя е дело на живот за тия, които я прегръщат И блажени са ония, които я държат.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
С мъдрост Господ основа земята, С разум утвърди небето.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
Чрез Неговото знание се разтвориха бездните И от облаците капе роса.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Сине мой, тоя неща да се не отдалечават от очите ти; Пази здравомислие и разсъдителност,
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Така те ще бъдат живот на душата ти И украшение на шията ти.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Тогава ще ходиш безопасно по пътя си, И ногата ти не ще се спъне.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Когато лягаш не ще се страхуваш; Да! ще лягаш и сънят ти ще бъде сладък.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Не ще се боиш от внезапен страх, Нито от бурята, когато нападне нечестивите,
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Защото Господ ще бъде твое упование, И ще пази ногата то да се не хване.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Не въздържай доброто от ония, на които се дължи, Когато ти дава ръка да им го направиш.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Не казвай на ближния си: Иди върни се пак, И ще ти дам утре, Когато имаш при себе си това, което му се пада.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Не измисляй зло против ближния си, Който с увереност живее при тебе.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Не се карай с него без причина, Като не ти е направил зло.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Не завиждай на насилник човек, И не избирай ни един от пътищата му,
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Защото Господ се гнуси от опакия, Но интимно общува с праведните.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Проклетия от Господа има в дома на нечестивия; А Той благославя жилището на праведните.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Наистина Той се присмива на присмивачите. А на смирените дава благодат.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Мъдрите ще наследят слова, А безумните ще отнесат срам.