< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
Człowiek, który na częste karanie zatwardza kark swój, nagle zniszczeje, i nie wskóra.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
Gdy się rozmnażają sprawiedliwi, weseli się lud; ale gdy panuje bezbożnik, wzdycha lud.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
Mąż, który miłuje mądrość, uwesela ojca swego; ale kto chowa nierządnicę, traci majętność.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
Król sądem ziemię utwierdza; ale mąż, który dary bierze, podwraca ją.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
Człowiek, który pochlebia przyjacielowi swemu, rozciąga sieć przed nogami jego.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
Występek złego jest mu sidłem; ale sprawiedliwy śpiewa i weseli się.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
Sprawiedliwy wyrozumiewa sprawę nędznych; ale niezbożnik nie ma na to rozumu i umiejętności.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Mężowie naśmiewcy zawodzą miasto; ale mądrzy odwracają gniew.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
Mąż mądry, wiedzieli spór z mężem głupim, choćby się gniewał, choćby się też śmiał, nie będzie miał pokoju.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Mężowie krwawi nienawidzą uprzejmego; ale uprzejmi staranie wiodą o duszę jego.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
Wszystkiego ducha swego wywiera głupi, ale mądry na dalszy czas go zawściąga.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
Pana, który rad słucha słów kłamliwych, wszyscy słudzy jego są niepobożni.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
Ubogi i zdzierca spotkali się; a wszakże obydwóch oczy Pan oświeca.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
Króla, który sądzi uciśnionych według prawdy, stolica jego na wieki utwierdzona będzie.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
Rózga i karność mądrość daje; ale dziecię swawolne zawstydza matkę swoję.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
Gdy się rozmnażają niezbożni, rozmnaża się i przestępstwo; ale sprawiedliwi upadek ich oglądają.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Karz syna twego, a sprawić odpocznienie, i sposobi rozkosz duszy twojej.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Gdy proroctwo ustaje, lud bywa rozproszony; ale kto strzeże zakonu, błogosławiony jest.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
Sługa nie bywa słowami naprawiony; bo choć rozumie, jednak nie odpowiada.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Ujrzysz człowieka skwapliwego w sprawach swoich; ale lepsza jest nadzieja o głupim, niż o nim.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
Kto w rozkoszy chowa z dzieciństwa sługę swego, na ostatek będzie chciał być za syna.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
Człowiek gniewliwy wszczyna zwadę, a pierzchliwy wiele grzeszy.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
Pycha człowiecza poniża go; ale pokorny w duchu sławy dostępuje.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Kto spółkuje ze złodziejem, ma w nienawiści duszę swoję; także też kto przeklęstwa słyszy, a nie objawia go.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
Strach człowieczy stawia sobie sidło; ale kto ma nadzieję w Panu, wywyższony będzie.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Wiele tych, co szukają twarzy panów; aleć od Pana jest sąd każdego.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
Sprawiedliwym jest mąż niezbożny obrzydliwością; a zasię kto w uprzejmości chodzi, jest niezbożnym obrzydliwością.

< Miyambo 29 >