< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
Vīrs, kas pārmācīts, tomēr ciets, taps piepeši salauzts, un nebūs, kas dziedina.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
Kad taisnie iet vairumā, tad ļaudis priecājās; bet kad bezdievīgais valda, tad ļaudis nopūšās.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
Kas gudrību mīļo, iepriecina savu tēvu; bet kas ar maukām pinās, tas izplītē savu mantu.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
Caur tiesu un taisnību ķēniņš dara valsti pastāvam; bet kas dāvanas plēš, tas to izposta.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
Kas otram mīksti pieglaužas, met tīklu viņa soļiem.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
Bezdievīgais savaldzinājās savos grēkos, bet taisnais priecājās un līksmojās.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
Taisnais ņem vērā nabaga žēlošanos; bezdievīgais par to nemaz nebēdā.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Kam viss tik smiekls, sakurina pilsētu; bet gudrie apslāpē kaislību.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
Gudrs ar ģeķi pie tiesas, tad skaistās, tad smejas, galā netiek.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Asins vīri ienīst bezvainīgo, bet taisnie rūpējās par viņa dvēseli.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
Ģeķis izkrata visu savu padomu, bet gudrs vīrs to patur pie sevis.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
Kungs, kas uz meliem klausa, tam visi kalpi blēži.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
Nabagi un mantas plēsēji sastop viens otru; abiem Tas Kungs dod acu gaismu.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
Ķēniņš, kas nabagiem nes taisnu tiesu, tā goda krēsls pastāvēs mūžīgi.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
Rīkste un pārmācība dod gudrību; bet bērns savā vaļā dara mātei kaunu.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
Kur bezdievīgie iet vairumā, tur vairojās grēki; bet taisnie redzēs viņu krišanu.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Pārmāci savu dēlu, tad tev būs prieks no viņa un tavai dvēselei līksmība.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Kur Dieva mācības nav, tur ļaudis nevaldāmi; bet svētīgs, kas mācību sargā.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
Kalps ar vārdiem nav mācams; lai gan labi prot, taču neklausa,
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Kad tu vīru redzi, kam veikla mēle, tad no muļķa vairāk cerības nekā no tāda.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
Kad kalpu no pirmā gala izlutina, tad pēcgalā grib būt par pašu dēlu.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
Ātrs cilvēks saceļ bāršanos, un sirdīgs vīrs padara daudz grēku.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
Cilvēka lepnība viņu gāzīs, bet pazemīgs gars panāks godu.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Kas ar zagli dalās, tas ienīst savu dvēseli; viņš dzird Dieva lāstus un nepierāda.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
Priekš cilvēkiem drebēt ieved valgos; bet kas uz To Kungu paļaujas, ir drošā vietā.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Daudzi meklē valdnieka vaigu; bet no Tā Kunga nāk katram tā tiesa.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
Netaisnais riebj taisniem, un kas bezvainīgs savā ceļā, riebj bezdievīgam.

< Miyambo 29 >