< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
He who is often rebuked and stiffens his neck will be destroyed suddenly, with no remedy.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
When the righteous thrive, the people rejoice; but when the wicked rule, the people groan.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
Whoever loves wisdom brings joy to his father; but a companion of prostitutes squanders his wealth.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
The king by justice makes the land stable, but he who takes bribes tears it down.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
A man who flatters his neighbour spreads a net for his feet.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
An evil man is snared by his sin, but the righteous can sing and be glad.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
The righteous care about justice for the poor. The wicked aren’t concerned about knowledge.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Mockers stir up a city, but wise men turn away anger.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
If a wise man goes to court with a foolish man, the fool rages or scoffs, and there is no peace.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
The bloodthirsty hate a man of integrity; and they seek the life of the upright.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
A fool vents all of his anger, but a wise man brings himself under control.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
If a ruler listens to lies, all of his officials are wicked.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
The poor man and the oppressor have this in common: The LORD gives sight to the eyes of both.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
The king who fairly judges the poor, his throne shall be established forever.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
The rod of correction gives wisdom, but a child left to himself causes shame to his mother.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
When the wicked increase, sin increases; but the righteous will see their downfall.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Correct your son, and he will give you peace; yes, he will bring delight to your soul.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Where there is no revelation, the people cast off restraint; but one who keeps the law is blessed.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
A servant can’t be corrected by words. Though he understands, yet he will not respond.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Do you see a man who is hasty in his words? There is more hope for a fool than for him.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
He who pampers his servant from youth will have him become a son in the end.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
An angry man stirs up strife, and a wrathful man abounds in sin.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
A man’s pride brings him low, but one of lowly spirit gains honour.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Whoever is an accomplice of a thief is an enemy of his own soul. He takes an oath, but dares not testify.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
The fear of man proves to be a snare, but whoever puts his trust in the LORD is kept safe.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Many seek the ruler’s favour, but a man’s justice comes from the LORD.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
A dishonest man detests the righteous, and the upright in their ways detest the wicked.

< Miyambo 29 >