< Miyambo 29 >
1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
Člověk, kterýž často kárán bývaje, zatvrzuje šíji, rychle potřín bude, tak že neprospěje žádné lékařství.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
Když se množí spravedliví, veselí se lid; ale když panuje bezbožník, vzdychá lid.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
Muž, kterýž miluje moudrost, obveseluje otce svého; ale kdož se přitovaryšuje k nevěstkám, mrhá statek.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
Král soudem upevňuje zemi, muž pak, kterýž béře dary, boří ji.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
Člověk, kterýž pochlebuje příteli svému, rozprostírá sít před nohama jeho.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
Výstupek bezbožného jest jemu osídlem, spravedlivý pak prozpěvuje a veselí se.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
Spravedlivý vyrozumívá při nuzných, ale bezbožník nemá s to rozumnosti ani umění.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Muži posměvači zavozují město, ale moudří odvracují hněv.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
Muž moudrý, kterýž se nesnadní s mužem bláznivým, buď že se pohne, buď že se směje, nemá pokoje.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Vražedlníci v nenávisti mají upřímého, ale upřímí pečují o duši jeho.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
Všecken duch svůj vypouští blázen, ale moudrý na potom zdržuje jej.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
Pána toho, kterýž rád poslouchá slov lživých, všickni služebníci jsou bezbožní.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
Chudý a dráč potkávají se, obou dvou však oči osvěcuje Hospodin.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
Krále toho, kterýž soudí právě nuzné, trůn na věky bývá utvrzen.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
Metla a kárání dává moudrost, ale dítě sobě volné k hanbě přivodí matku svou.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
Když se rozmnožují bezbožní, rozmnožuje se převrácenost, a však spravedliví spatřují pád jejich.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Tresci syna svého, a přineseť odpočinutí, a způsobí rozkoš duši tvé.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Když nebývá vidění, rozptýlen bývá lid; kdož pak ostříhá zákona, blahoslavený jest.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
Slovy nebývá napraven služebník; nebo rozuměje, však neodpoví.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Spatřil-li bys člověka, an jest kvapný v věcech svých, lepší jest naděje o bláznu, než o takovém.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
Kdo rozkošně chová z dětinství služebníka svého, naposledy bude syn.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
Člověk hněvivý vzbuzuje svár, a prchlivý mnoho hřeší.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
Pýcha člověka snižuje jej, ale chudý duchem dosahuje slávy.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Kdo má spolek s zlodějem, v nenávisti má duši svou; zlořečení slyší, však neoznámí.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
Strašlivý člověk klade sobě osídlo, ale kdo doufá v Hospodina, bývá povýšen.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Mnozí hledají tváři pánů, ješto od Hospodina jest soud jednoho každého.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
Ohavností spravedlivým jest muž nepravý, ohavností pak bezbožnému, kdož upřímě kráčí.